< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
Чел рэу фуӂе фэрэ сэ фие урмэрит, дар чел неприхэнит ындрэзнеште ка ун леу тынэр.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
Кынд есте рэскоалэ ынтр-о царэ, сунт мулць капь, дар ку ун ом причепут ши ынчеркат, домния дэйнуеште.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
Ун ом сэрак каре апасэ пе чей обиждуиць есте ка о рупере де норь каре адуче липсэ де пыне.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
Чей че пэрэсеск леӂя лаудэ пе чел рэу, дар чей че пэзеск леӂя се мыние пе ел.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Оамений дедаць ла рэу ну ынцелег че есте дрепт, дар чей че каутэ пе Домнул ынцелег тотул.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Май мулт прецуеште сэракул каре умблэ ын неприхэниря луй декыт богатул каре умблэ пе кэй сучите.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
Чел че пэзеште леӂя есте ун фиу причепут, дар чел че умблэ ку чей десфрынаць фаче рушине татэлуй сэу.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
Чине ышь ынмулцеште авуцииле прин добындэ ши камэтэ ле стрынӂе пентру чел че аре милэ де сэрачь.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
Дакэ чинева ышь ынтоарче урекя ка сэ н-аскулте леӂя, кяр ши ругэчуня луй есте о скырбэ.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
Чине рэтэчеште пе оамений фэрэ приханэ пе каля чя ря каде ын гроапа пе каре а сэпат-о, дар оамений фэрэ приханэ моштенеск феричиря.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
Омул богат се креде ынцелепт, дар сэракул каре есте причепут ыл черчетязэ.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
Кынд бируеск чей неприхэниць, есте о маре славэ, дар кынд се ыналцэ чей рэй, фиекаре се аскунде.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
Чине ышь аскунде фэрэделеӂиле ну пропэшеште, дар чине ле мэртурисеште ши се ласэ де еле капэтэ ындураре.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Фериче де омул каре се теме неконтенит, дар чел че-шь ымпетреште инима каде ын ненорочире.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
Ка ун леу каре рэкнеште ши ка ун урс флэмынд, аша есте чел рэу каре стэпынеште песте ун попор сэрак.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
Ун воевод фэрэ причепере ышь ынмулцеште фаптеле де асуприре, дар чел че урэште лэкомия ышь лунӂеште зилеле.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
Ун ом ал кэруй куӂет есте ынкэркат ку сынӂеле алтуя фуӂе пынэ ла гроапэ: нимень сэ ну-л опряскэ.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
Чине умблэ ын неприхэнире гэсеште мынтуиря, дар чине умблэ пе доуэ кэй стрымбе каде ынтр-о гроапэ.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
Чине ышь лукрязэ кымпул аре белшуг де пыне, дар чине аляргэ дупэ лукрурь де нимик аре белшуг де сэрэчие.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
Ун ом крединчос есте нэпэдит де бинекувынтэрь, дар чел че вря сэ се ымбогэцяскэ репеде ну рэмыне непедепсит.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
Ну есте бине сэ кауць ла фаца оаменилор; кяр пентру о букатэ де пыне поате ун ом сэ се дедя ла пэкат.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
Ун ом пизмаш се грэбеште сэ се ымбогэцяскэ, ши ну штие кэ липса ва вени песте ел.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
Чине мустрэ пе алций гэсеште май мултэ бунэвоинцэ пе урмэ декыт чел ку лимба лингушитоаре.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
Чине фурэ пе татэл сэу ши пе мама са ши зиче кэ ну есте ун пэкат есте товарэш ку нимичиторул.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
Чел лаком стырнеште чертурь, дар чел че се ынкреде ын Домнул есте сэтурат дин белшуг.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
Чине се ынкреде ын инима луй есте ун небун, дар чине умблэ ын ынцелепчуне ва фи мынтуит.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
Чине дэ сэракулуй ну дуче липсэ, дар чине ынкиде окий есте ынкэркат ку блестеме.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
Кынд се ыналцэ чей рэй, фиекаре се аскунде, дар кынд пер ей, чей бунь се ынмулцеск.

< Miyambo 28 >