< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
Bezdievīgais bēg, kur dzinēja nav; bet taisnie ir droši, kā jauns lauva.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
Caur dumpjiem zemei tiek daudz valdnieku; bet ja ļaudis prātīgi un apdomīgi, tad valdnieks paliek ilgi.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
Nabaga kungs, kas nabagus apspiež, ir kā plūdu lietus, un maizes nav.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
Kas paši mācību atstāj, tie slavē bezdievīgus; bet kas mācību tura, tie ļaunojās par tiem.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Ļauni ļaudis neatzīst, kas Dieva tiesa, bet kas To Kungu meklē, tie atzīst visu.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Labāks ir nabags, kas staigā skaidrībā, nekā bagāts netiklā ceļā.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
Kas glabā mācību, tas ir prātīgs bērns; bet kas rijēju biedrs, dara tēvam kaunu.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
Kas savu mantu vairo ar augļošanu un augļus ņemot, tas to krāj tādam, kas par nabagiem apžēlojās.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
Kas savu ausi nogriež no Dieva bauslības, pat tāda cilvēka lūgšana ir neganta.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
Kas maldina bezvainīgus uz ļauniem ceļiem, tas pats kritīs savā bedrē; bet tie sirdsskaidrie iemantos labumu.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
Bagāts vīrs savā prātā gudrs; bet nabags, kas prātīgs, to izmana.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
Kad taisnie gavilē, tas ir liels jaukums; bet kad bezdievīgie galvu paceļ tad ļaudis slēpjas.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
Kas savus pārkāpumus apklāj, tam tas neizdosies; bet kas tos izsūdz un atstāj, tas dabūs žēlastību.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Svētīgs, kas Dievu bīstas vienmēr; bet kas savu sirdi apcietina, kritīs postā.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
Bezdievīgais, kas valda pār nabaga ļaudīm, ir rūkdams lauva un izsalcis lācis.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
Valdnieks nav gudrs, ja mudīgs uz varas darbiem; bet kas labprāt neplēš, dzīvos ilgi.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
Pie kā rokām cilvēka asinis līp, tas bēgs līdz bedrei; palīga tas nedabūs.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
Kas staigā vientiesībā, tam labi klāsies; bet blēdis pa diviem ceļiem vienā klups.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
Kas savu zemi kopj, būs maizes paēdis; bet kas niekus triec, būs bada paēdis.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
Godīgs vīrs būs bagāti svētīts, bet kas dzenās bagāts palikt, nebūs nenoziedzīgs.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
Nav labi, cilvēka vaigu uzlūkot; jo tāds arī par maizes kumosu dara netaisnību.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
Kas ar skaudīgu aci dzenās pēc bagātības, neapdomā, ka viņam trūcība pienāks.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
Kas cilvēku aprāj, tas pēc atradīs vairāk pateicības, nekā tāds, kam mīksta mēle.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
Kas savu tēvu vai māti laupa un saka: „Tas nav grēks!“tāds ir slepkavas biedrs.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
Negausis saceļ nemieru; bet kas uz To Kungu cerē, tas būs turīgs.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
Kas uz savu sirdi paļaujas, ir ģeķis; bet kas ar gudrību staigā, tiks izglābts.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
Kas nabagam dod, tam nepietrūks; bet kas savas acis priekš tā aizslēdz, tam uzies daudz lāstu.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
Kad bezdievīgie paceļ galvu, tad ļaudis slēpjas; bet kad tie beigti, tad taisnie iet vairumā.

< Miyambo 28 >