< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
THE wicked flee when no man pursueth: but the righteous are bold as a lion.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
For the transgression of a land many are the princes thereof: but by a man of understanding and knowledge the state thereof shall be prolonged.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
A poor man that oppresseth the poor is like a sweeping rain which leaveth no food.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
They that forsake the law praise the wicked: but such as keep the law contend with them.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Evil men understand not judgment: but they that seek the Lord understand all things.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Better is the poor that walketh in his uprightness, than he that is perverse in his ways, though he be rich.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
Whoso keepeth the law is a wise son: but he that is a companion of riotous men shameth his father.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
He that by usury and unjust gain increaseth his substance, he shall gather it for him that will pity the poor.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
He that turneth away his ear from hearing the law, even his prayer shall be abomination.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
Whoso causeth the righteous to go astray in an evil way, he shall fall himself into his own pit: but the upright shall have good things in possession.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
The rich man is wise in his own conceit; but the poor that hath understanding searcheth him out.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
When righteous men do rejoice, there is great glory: but when the wicked rise, a man is hidden.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
He that covereth his sins shall not prosper: but whoso confesseth and forsaketh them shall have mercy.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Happy is the man that feareth alway: but he that hardeneth his heart shall fall into mischief.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
As a roaring lion, and a ranging bear; so is a wicked ruler over the poor people.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
The prince that wanteth understanding is also a great oppressor: but he that hateth covetousness shall prolong his days.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
A man that doeth violence to the blood of any person shall flee to the pit; let no man stay him.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
Whoso walketh uprightly shall be saved: but he that is perverse in his ways shall fall at once.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
He that tilleth his land shall have plenty of bread: but he that followeth after vain persons shall have poverty enough.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
A faithful man shall abound with blessings: but he that maketh haste to be rich shall not be innocent.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
To have respect of persons is not good: for for a piece of bread that man will transgress.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
He that hasteth to be rich hath an evil eye, and considereth not that poverty shall come upon him.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
He that rebuketh a man afterwards shall find more favour than he that flattereth with the tongue.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
Whoso robbeth his father or his mother, and saith, It is no transgression; the same is the companion of a destroyer.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
He that is of a proud heart stirreth up strife: but he that putteth his trust in the Lord shall be made fat.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
He that trusteth in his own heart is a fool: but whoso walketh wisely, he shall be delivered.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
He that giveth unto the poor shall not lack: but he that hideth his eyes shall have many a curse.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
When the wicked rise, men hide themselves: but when they perish, the righteous increase.

< Miyambo 28 >