< Miyambo 28 >

1 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
Opaki bježe i kad ih nitko ne progoni, a pravednici su neustrašivi kao mladi lav.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
Kad se u zemlji griješi, mnogi su joj knezovi, a s čovjekom razumnim i umnim uprava je postojana.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
Čovjek opak koji tlači ubogoga - kiša je razorna poslije koje kruha nema.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
Koji zapuštaju Zakon, veličaju opake, a koji se drže Zakona, protive im se.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
Zli ljudi ne razumiju pravice, a koji traže Jahvu, razumiju sve.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
Bolji je siromah koji živi bezazleno nego bogataš koji kroči krivim putem.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
Tko se drži Zakona, razuman je sin, a tko se druži s izbjeglicama, sramoti oca svoga.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
Tko umnožava bogatstvo svoje lihvom i pridom, skuplja ga onomu tko je milostiv ubogima.
9 Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
Tko uklanja uho svoje da ne sluša Zakona, i molitva je njegova mrska.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
Tko zavodi poštene na put zao, past će u jamu svoju, a pošteni će baštiniti sreću.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
Bogat se čovjek čini sebi mudrim, ali će ga razuman siromah raskrinkati.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
Velika je slava kad se raduju pravednici, a kad se dižu opaki, ljudi se kriju.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
Tko skriva svoje grijehe, nema sreće, a tko ih ispovijeda i odriče ih se, milost nalazi.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
Blago čovjeku uvijek bojaznu, jer čovjek okorjela srca zapada u nesreću.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
Lav koji riče i gladan medvjed: takav je opak vladalac siromašnu narodu.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
Nerazuman knez čini mnoga nasilja, a koji mrzi lakomost, dugo živi.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
Onaj koga tišti krvna krivica, do groba bježi: ne zaustavljajte ga.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
Spasava se tko živi pravedno, tko se koleba između dva puta, propada na jednom od njih.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
Tko obrađuje svoju zemlju, nasitit će se kruha, a tko trči za tlapnjama, nasitit će se siromaštva.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
Čestit čovjek stječe blagoslov, a tko hrli za bogatstvom, ne ostaje bez kazne.
21 Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
Ne valja biti pristran na sudu, jer i za zalogaj kruha čovjek čini zlo.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
Pohlepnik hrli za bogatstvom, a ne zna da će ga stići oskudica.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
Tko kori čovjeka, nalazi poslije veću milost nego onaj koji laska jezikom.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
Tko pljačka oca svoga i majku svoju i veli: “Nije grijeh”, drug je razbojniku.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
Lakomac zameće svađu, a tko se uzda u Jahvu, uspjet će.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
Bezuman je tko se uzda u svoje srce, a spasava se tko živi mudro.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
Tko daje siromahu, ne trpi oskudicu; a tko odvraća oči svoje, bit će proklet.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
Kad se dižu opaki, ljudi se kriju, a kad propadaju, tad se množe pravednici.

< Miyambo 28 >