< Miyambo 27 >
1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
No te jactes del mañana; porque no sabes lo que puede traer un día.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Que otro hombre te alabe, y no su propia boca; un extraño, y no tus propios labios.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Una piedra es pesada, y la arena es una carga; pero la provocación de un tonto es más pesada que ambas.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
La ira es cruel, y la ira es abrumadora; pero, ¿quién es capaz de enfrentarse a los celos?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Mejor es la reprimenda abierta que el amor oculto.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Las heridas de un amigo son fieles, aunque los besos de un enemigo sean profusos.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Un alma llena aborrece un panal; pero para un alma hambrienta, todo lo amargo es dulce.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Como un pájaro que se aleja de su nido, así es un hombre que se aleja de su hogar.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
El perfume y el incienso alegran el corazón; también lo hace el consejo sincero de un amigo.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
No abandones a tu amigo y al amigo de tu padre. No vayas a la casa de tu hermano en el día de tu desastre. Un vecino cercano es mejor que un hermano lejano.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Sé sabio, hijo mío, y trae alegría a mi corazón, entonces puedo responder a mi atormentador.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
Un hombre prudente ve el peligro y se refugia; pero los simples pasan, y sufren por ello.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Toma su prenda cuando pone una garantía para un extranjero. ¡Sosténgalo por una mujer caprichosa!
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
El que bendice a su prójimo en voz alta por la mañana, será tomado como una maldición por él.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Una gota continua en un día de lluvia y una esposa contenciosa son iguales:
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
contenerla es como contener el viento, o como agarrar aceite en su mano derecha.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
El hierro afila el hierro; así un hombre agudiza el semblante de su amigo.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
El que cuide la higuera comerá su fruto. El que cuida a su amo será honrado.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Como el agua refleja un rostro, por lo que el corazón de un hombre refleja al hombre.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
El Seol y Abadón nunca están satisfechos; y los ojos de un hombre nunca están satisfechos. (Sheol )
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
El crisol es para la plata, y el horno para el oro; pero el hombre es refinado por su alabanza.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Aunque muelas a un tonto en un mortero con un pilón junto con el grano, sin embargo, no se le quitará su necedad.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Conoce bien el estado de tus rebaños, y presta atención a tus rebaños,
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
porque las riquezas no son eternas, ni la corona perdura en todas las generaciones.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Se quita el heno y aparece el nuevo crecimiento, los pastos de las colinas se recogen.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Los corderos son para tu ropa, y las cabras son el precio de un campo.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
Allíhabrá mucha leche de cabra para su alimentación, para la alimentación de su familia, y para la alimentación de sus sirvientas.