< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ну те фэли ку зиуа де мыне, кэч ну штий че поате адуче о зи!
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Сэ те лауде алтул, ну гура та, ун стрэин, ну бузеле тале!
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Пятра есте гря ши нисипул есте греу, дар супэраря пе каре о причинуеште небунул есте май гря декыт амындоуэ.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Фурия есте фэрэ милэ ши мыния, нэвалникэ, дар чине поате ста ымпотрива ӂелозией?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Май бине о мустраре пе фацэ декыт о приетение аскунсэ.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Рэниле фэкуте де ун приетен доведеск крединчошия луй, дар сэрутэриле унуй врэжмаш сунт минчиноасе.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Сэтулул калкэ ын пичоаре фагуреле де мьере, дар пентру чел флэмынд тоате амэрэчуниле сунт дулчь.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Ка пасэря плекатэ дин куйбул ей, аша есте омул плекат дин локул сэу.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Кум ынвеселеск унтделемнул ши тэмыя инима, аша де дулчь сунт сфатуриле плине де драгосте але унуй приетен.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Ну пэрэси пе приетенул тэу ши пе приетенул татэлуй тэу, дар ну интра ын каса фрателуй тэу ын зиуа неказулуй тэу: май бине ун вечин апроапе декыт ун фрате департе.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Фиуле, фий ынцелепт ши ынвеселеште-мь инима, ши атунч вой путя рэспунде челуй че мэ батжокореште!
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
Омул кибзуит веде рэул ши се аскунде, дар проштий мерг спре ел ши сунт педепсиць.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Я-й хайна, кэч с-а пус кезаш пентру алтул, я-л зэлог ын локул уней стрэине!
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Бинекувынтаря апроапелуй ку глас таре дис-де-диминяцэ есте привитэ ка ун блестем.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
О стряшинэ, каре пикурэ некурмат ынтр-о зи де плоае, ши о невастэ гылчевитоаре сунт тот уна.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Чине о опреште паркэ опреште вынтул ши паркэ цине унтделемнул ын мына дряптэ.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Дупэ кум ферул аскуте ферул, тот аша ши омул ацыцэ мыния алтуй ом.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Чине ынгрижеште де ун смокин ва мынка дин родул луй ши чине-шь пэзеште стэпынул ва фи прецуит.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Кум рэспунде ын апэ фаца ла фацэ, аша рэспунде инима омулуй инимий омулуй.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Дупэ кум Локуинца морцилор ши адынкул ну се пот сэтура, тот аша нич окий омулуй ну се пот сэтура. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
Че есте тигая пентру лэмуриря арӂинтулуй ши купторул пентру лэмуриря аурулуй, ачея есте бунул нуме пентру ун ом.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Пе небун, кяр дакэ л-ай писа ку писэлогул ын пиуэ, ын мижлокул грэунцелор, небуния тот н-ар еши дин ел.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Ынгрижеште бине де оиле тале ши я сяма ла турмеле тале!
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Кэч ничо богэцие ну цине вешник ши нич кунуна ну рэмыне пе вечие.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Дупэ че се ридикэ фынул, се аратэ вердяца ноуэ, ши ербуриле де пе мунць сунт стрынсе.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Меий сунт пентру ымбрэкэминте ши цапий, пентру плата огорулуй;
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
лаптеле капрелор ць-ажунӂе пентру храна та, а касей тале ши пентру ынтрецинеря служничелор тале.

< Miyambo 27 >