< Miyambo 27 >
1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Não presumas do dia de amanhã, porque não sabes o que parirá o dia.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Louve-te o estranho, e não a tua boca, o estrangeiro e não os teus lábios.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Pesada é a pedra, e a areia é carregada; porém a ira do insensato é mais pesada do que elas ambas.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Cruel é o furor e a impetuosa ira, mas quem parará perante a inveja?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Melhor é a repreensão aberta do que o amor encoberto.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Fieis são as feridas feitas pelo que ama, mas os beijos do que aborrece são enganosos.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
A alma farta piza o favo de mel, mas à alma faminta todo o amargo é doce.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Qual é a ave que vagueia do seu ninho, tal é o homem que anda vagueando do seu lugar.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
O óleo e o perfume alegram o coração: assim a doença do amigo de alguém com o conselho cordial.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Não deixes a teu amigo, nem ao amigo de teu pai, nem entres na casa de teu irmão no dia da tua adversidade: melhor é o vizinho de perto do que o irmão ao longe.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Sê sábio, filho meu, e alegra o meu coração; para que tenha alguma coisa que responder àquele que me desprezar.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
O avisado vê o mal, e esconde-se; mas os simples passam e pagam a pena.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Quando alguém fica por fiador do estranho, toma-lhe tu a sua roupa; e o penhora pela estranha.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
O que bendiz ao seu amigo em alta voz, madrugando pela manhã, por maldição se lhe contará.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
O gotejar contínuo no dia de grande chuva, e a mulher contenciosa, uma e outra são semelhantes.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Todos os que a esconderem esconderão o vento: e o óleo da sua dextra clama.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Como o ferro com o ferro se aguça, assim o homem aguça o rosto do seu amigo.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
O que guarda a figueira comerá do seu fruto; e o que atenta para seu senhor, será honrado.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Como na água o rosto corresponde ao rosto, assim o coração do homem ao homem.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
Como o inferno e a perdição nunca se fartam, assim os olhos do homem nunca se fartam. (Sheol )
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
Como o crisol é para a prata, e o forno para o ouro, assim se prova o homem pelos louvores.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Ainda quando pizares o tolo com uma mão de gral entre grãos de cevada pilada, não se irá dele a sua estultícia.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Procura conhecer o estado das tuas ovelhas: põe o teu coração sobre o gado.
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Porque o tesouro não dura para sempre: ou durará a coroa de geração em geração?
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Quando se mostrar a erva, e aparecerem os renovos, então ajunta as hervas dos montes.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Os cordeiros serão para te vestires, e os bodes para o preço do campo.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
E a abastança do leite das cabras para o teu sustento, para sustento da tua casa, e para sustento das tuas criadas.