< Miyambo 27 >
1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
なんぢ明日のことを誇るなかれ そは一日の生ずるところの如何なるを知ざればなり
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
汝おのれの口をもて自ら讃むることなく人をして己を讃めしめよ 自己の口唇をもてせず 他人をして己をほめしめよ
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
石は重く沙は軽からず 然ど愚なる者の怒はこの二よりも重し
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
忿怒は猛く憤恨は烈し されど嫉妬の前には誰か立ことをを得ん
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
明白に譴むるに秘に愛するに愈る
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
愛する者の傷つくるは眞實よりし 敵の接吻するは偽詐よりするなり
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
飽るものは蜂の蜜をも踐つく されど饑たる者には苦き物さへもすべて甘し
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
その家を離れてさまよふ人は その巣を離れてさまよふ鳥のごとし
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
膏と香とは人の心をよろこばすなり 心よりして勸言を與ふる友の美しきもまた斯のごとし
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
なんぢの友と汝の父の友とを棄るなかれ なんぢ患難にあふ日に兄弟の家にいることなかれ 親しき隣は疏き兄弟に愈れり
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
わが子よ智慧を得てわが心を悦ばせよ 然ば我をそしる者に我こたふることを得ん
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
賢者は禍害を見てみづから避け 拙者はすすみて罰をうく
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
人の保證をなす者よりは先その衣をとれ 他人の保證をなす者をば固くとらへよ
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
晨はやく起て大聲にその鄰を祝すれば却て呪詛と見なされん
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
相爭ふ婦は雨ふる日に絶ずある雨漏のごとし
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
これを制ふるものは風をおさふるがごとく 右の手に膏をつかむがごとし
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
鐵は鐵をとぐ 斯のごとくその友の面を研なり
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
無花果の樹をまもる者はその果をくらふ 主を貴ぶものは譽を得
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
水に照せば面と面と相肖るがごとく 人の心は人の心に似たり
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
陰府と沈淪とは飽ことなく 人の目もまた飽ことなし (Sheol )
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
坩堝によりて銀をためし鑢によりて金をためし その讃らるる所によりて人をためす
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
なんぢ愚なる者を臼にいれ杵をもて麥と偕にこれを搗ともその愚は去らざるなり
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
なんぢの羊の情况をよく知り なんぢの群に心を留めよ
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
富は永く保つものにあらず いかで位は世々にたもたん
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
艸枯れ苗いで山の蔬菜あつめらる
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
羔羊はなんぢの衣服を出し 牝羊は田圃を買ふ價となり
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
牝羊の乳はおほくして汝となんぢの家人の糧となり汝の女をやしなふにたる