< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ne te vante point du jour du lendemain; car tu ne sais pas ce que ce jour peut enfanter.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Qu'un autre te loue, et non pas ta propre bouche; que ce soit un étranger, et non tes lèvres.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
La pierre est pesante, et le sable est lourd; mais la colère d'un insensé est plus pesante que l'un et l'autre.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
La colère est cruelle; et la fureur est comme une inondation; mais qui pourra subsister devant la jalousie?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Une réprimande ouverte vaut mieux qu'une amitié cachée.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Les blessures faites par celui qui aime, sont fidèles; mais les baisers de celui qui hait sont trompeurs.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Celui qui est rassasié, foule aux pieds les rayons de miel; mais celui qui a faim trouve doux même ce qui est amer.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Tel qu'est un oiseau qui erre loin de son nid, tel est l'homme qui s'éloigne de sa demeure.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
L'huile et le parfum réjouissent le cœur; telle est la douceur d'un ami dont le conseil vient du cœur.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Ne quitte point ton ami, ni l'ami de ton père, et ne va point dans la maison de ton frère au jour de ta détresse; car un bon voisin qui est près, vaut mieux qu'un frère qui est loin.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Mon fils, sois sage, et réjouis mon cœur, et je pourrai répondre à celui qui me fera des reproches.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
L'homme bien avisé prévoit le mal, et se met à l'abri; mais les simples passent outre et en portent la peine.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Quand quelqu'un aura cautionné un étranger, prends son vêtement; exige de lui un gage, à cause des étrangers.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Celui qui bénit son ami à haute voix, de bon matin, sera considéré comme s'il le maudissait.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Une gouttière continuelle au temps d'une grosse pluie, et une femme querelleuse, c'est tout un.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Qui veut la retenir essaie d'arrêter le vent et de saisir de l'huile de sa main.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Comme le fer aiguise le fer, ainsi un homme en aiguise un autre.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Celui qui garde le figuier, mangera de son fruit; ainsi celui qui garde son maître sera honoré.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Comme dans l'eau le visage répond au visage, ainsi le cœur d'un homme répond à celui d'un autre homme.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Le Sépulcre et le gouffre ne sont jamais rassasiés; de même, les yeux de l'homme sont insatiables. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
L'argent est éprouvé par le fourneau, l'or par le creuset; et l'homme est jugé d'après sa renommée.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Quand tu pilerais un insensé dans un mortier, parmi du grain, avec un pilon, sa folie ne se détacherait pas de lui.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Applique-toi à connaître l'état de tes brebis et donne tes soins à tes troupeaux.
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Car les richesses ne durent pas toujours, et la couronne ne demeure pas d'âge en âge.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Le foin se récolte, et la verdure paraît, et les herbes des montagnes sont recueillies.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Les agneaux seront pour te vêtir, et les boucs pour payer le champ.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
Et l'abondance du lait des chèvres sera pour ta nourriture, pour la nourriture de ta maison, et pour la vie de tes servantes.

< Miyambo 27 >