< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ne te félicite pas du jour de demain, car tu ne sais ce que peut apporter chaque jour.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Qu’un autre fasse ton éloge et non ta propre bouche; un étrangers et non tes lèvres à toi.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Lourde est la pierre, pesant le sable; mais le dépit d’un sot pèse plus lourd que les deux.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Cruelle est la colère, violent le courroux; mais qui peut tenir devant la jalousie?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Mieux vaut une réprimande ouverte qu’une amitié qui se dérobe.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Les blessures faites par un ami sont preuve d’affection, un ennemi est prodigue de caresses.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
La satiété fait fi du miel; la faim trouve doux ce qui est amer.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Comme l’oiseau qui erre loin de son nid, tel est l’homme qui erre loin de son pays.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Huile et parfum réjouissent le cœur; de même la bonté suave d’un ami qui donne de sincères conseils.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
N’Abandonne ni ton ami ni l’ami de ton père, ne franchis pas le seuil de ton frère au jour de ton malheur; mieux vaut un voisin qui est près de toi qu’un frère qui se tient à l’écart.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Sois sage, mon fils, tu réjouiras mon cœur, et j’aurai de quoi répliquer à qui m’insulte.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
L’Homme avisé aperçoit le danger et se met à l’abri; les niais passent outre et en pâtissent.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Il s’est porté garant pour un autre: saisis son vêtement; il a cautionné une étrangère: nantis-toi de son gage!
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Assourdir de grand matin son prochain par de bruyants saluts, c’est comme si on lui disait des injures.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Une gouttière qui se déverse par un jour d’orage et une femme acariâtre, c’est tout un.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Vouloir la retenir, c’est retenir le vent ou recueillir de l’huile dans sa main.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Le fer devient poli au contact du fer et l’homme au contact de son prochain.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Qui veille sur le figuier jouira de ses fruits qui veine sur son maître recueillera de l’honneur.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Comme dans l’eau le visage répond au visage, ainsi chez les hommes les cœurs se répondent.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Cheol et abîme sont insatiables; les yeux de l’homme le sont également. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
La fournaise, pour l’argent, le creuset pour l’or, et l’homme est prisé d’après sa réputation.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Tu broierais le sot dans un mortier avec le pilon, comme on fait des graines, que sa sottise ne se détacherait pas de lui.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Tâche de bien connaître l’état de tes brebis, porte ton attention sur tes troupeaux.
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Car les biens ne dureront pas toujours: les dignités se transmettent-elles de génération en génération?
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Que la végétation se fasse jour, que la verdure apparaisse, que les herbes des hauteurs soient recueillies,
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
et tu auras des brebis pour te vêtir, des béliers pour payer le prix d’un champ,
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
du lait de chèvres en abondance, pour te nourrir toi et ta famille et faire vivre tes domestiques.

< Miyambo 27 >