< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ne te glorifie pas du lendemain, car tu ne sais pas ce qu’enfantera le jour suivant.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Qu’un autre te loue, et non ta bouche; un étranger, et non tes lèvres.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
La pierre est lourde et le sable est pesant: plus que l’un et l’autre pèse la colère de l’insensé.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
La fureur est cruelle et la colère impétueuse; mais qui pourra tenir devant la jalousie?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Mieux vaut une réprimande ouverte qu’une amitié cachée.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Les blessures d’un ami sont inspirées par la fidélité, mais les baisers d’un ennemi sont trompeurs.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Celui qui est rassasié foule aux pieds le rayon de miel, mais à celui qui a faim tout ce qui est amer paraît doux.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Comme l’oiseau qui erre loin de son nid, ainsi l’homme qui erre loin de son lieu.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
L’huile et les parfums réjouissent le cœur; telle la douceur d’un ami dont le conseil vient du cœur.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
N’abandonne pas ton ami et l’ami de ton père, et n’entre pas dans la maison de ton frère au jour de ta détresse; mieux vaut un voisin proche qu’un frère éloigné.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Mon fils, deviens sage et réjouis mon cœur, afin que je puisse répondre à celui qui m’outrage.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
L’homme prudent voit le mal et se cache; les simples passent et en portent la peine.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Prends son vêtement, car il a répondu pour autrui; demande des gages à cause des étrangers.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Bénir son prochain à haute voix et de grand matin est réputé comme une malédiction.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Une gouttière continue dans un jour de pluie et une femme querelleuse se ressemblent.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Celui qui la retient, retient le vent, et sa main saisit de l’huile.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Le fer aiguise le fer; ainsi un homme aiguise un autre homme.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Celui qui garde son figuier en mangera les fruits, et celui qui garde son maître sera honoré.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Comme dans l’eau le visage répond au visage, ainsi le cœur de l’homme répond à l’homme.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Le schéol et l’abîme ne sont jamais rassasiés, de même les yeux de l’homme ne sont jamais rassasiés. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
Le creuset est pour l’argent, et le fourneau pour l’or; que l’homme éprouve de même la louange qu’il reçoit!
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Quand tu pilerais l’insensé dans un mortier, comme on broie le grain, avec le pilon, sa folie ne se séparerait pas de lui.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Connais bien l’état de tes brebis, applique ton attention à ton troupeau;
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
car la richesse ne dure pas toujours, ni une couronne d’âge en âge.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Mais quand l’herbe a paru, que la verdure s’est montrée, que le foin des montagnes est recueilli,
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
tu as des agneaux pour te vêtir, des boucs pour payer un champ;
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
tu as en abondance le lait des chèvres, pour ta nourriture et celle de ta maison, et pour l’entretien de tes servantes.

< Miyambo 27 >