< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Boast not thyself of to-morrow, For thou knowest not what a day bringeth forth.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Let another praise thee, and not thine own mouth, A stranger, and not thine own lips.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
A stone [is] heavy, and the sand [is] heavy, And the anger of a fool Is heavier than they both.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Fury [is] fierce, and anger [is] overflowing, And who standeth before jealousy?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Better [is] open reproof than hidden love.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Faithful are the wounds of a lover, And abundant the kisses of an enemy.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
A satiated soul treadeth down a honeycomb, And [to] a hungry soul every bitter thing [is] sweet.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
As a bird wandering from her nest, So [is] a man wandering from his place.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Ointment and perfume rejoice the heart, And the sweetness of one's friend — from counsel of the soul.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Thine own friend, and the friend of thy father, forsake not, And the house of thy brother enter not In a day of thy calamity, Better [is] a near neighbour than a brother afar off.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Be wise, my son, and rejoice my heart. And I return my reproacher a word.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
The prudent hath seen the evil, he is hidden, The simple have passed on, they are punished.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Take his garment, when a stranger hath been surety, And for a strange woman pledge it.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Whoso is saluting his friend with a loud voice, In the morning rising early, A light thing it is reckoned to him.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
A continual dropping in a day of rain, And a woman of contentions are alike,
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Whoso is hiding her hath hidden the wind, And the ointment of his right hand calleth out.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Iron by iron is sharpened, And a man sharpens the face of his friend.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
The keeper of a fig-tree eateth its fruit, And the preserver of his master is honoured.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
As [in] water the face [is] to face, So the heart of man to man.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Sheol and destruction are not satisfied, And the eyes of man are not satisfied. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
A refining pot [is] for silver, and a furnace for gold, And a man according to his praise.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
If thou dost beat the foolish in a mortar, Among washed things — with a pestle, His folly turneth not aside from off him.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Know well the face of thy flock, Set thy heart to the droves,
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
For riches [are] not to the age, Nor a crown to generation and generation.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Revealed was the hay, and seen the tender grass, And gathered the herbs of mountains.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Lambs [are] for thy clothing, And the price of the field [are] he-goats,
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
And a sufficiency of goats' milk [is] for thy bread, For bread to thy house, and life to thy damsels!

< Miyambo 27 >