< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Boast not for tomorrow, for thou knowest not what the day to come may bring forth.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Let another praise thee, and not thy own mouth: a stranger, and not thy own lips.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
A stone is heavy, and sand weighty: but the anger of a fool is heavier than them both.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Anger hath no mercy, nor fury when it breaketh forth: and who can bear the violence of one provoked?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Open rebuke is better than hidden love.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Better are the wounds of a friend, than the deceitful kisses of an enemy.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
A soul that is full shall tread upon the honeycomb: and a soul that is hungry shall take even bitter for sweet.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
As a bird that wandereth from her nest, so is a man that leaveth his place.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Ointment and perfumes rejoice the heart: and the good counsels of a friend are sweet to the soul.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Thy own friend, and thy father’s friend forsake not: and go not into thy brother’s house in the day of thy affliction. Better is a neighbour that is near, than a brother afar off.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Study wisdom, my son, and make my heart joyful, that thou mayst give an answer to him that reproacheth.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
The prudent man seeing evil hideth himself: little ones passing on have suffered losses.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Take away his garment that hath been surety for a stranger: and take from him a pledge for strangers.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
He that blesseth his neighbour with a loud voice, rising in the night, shall be like to him that curseth.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Roofs dropping through in a cold day, and a contentious woman are alike.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
He that retaineth her, is as he that would hold the wind, and shall call in the oil of his right hand.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Iron sharpeneth iron, so a man sharpeneth the countenance of his friend.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
He that keepeth the fig tree, shall eat the fruit thereof: and he that is the keeper of his master, shall be glorified.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
As the faces of them that look therein, shine in the water, so-the hearts of men are laid open to the wise.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Hell and destruction are never filled: so the eyes of men are never satisfied. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
As silver is tried in the fining-pot and gold in the furnace: so a man is tried by the mouth of him that praiseth. The heart of the wicked seeketh after evils, but the righteous heart seeketh after knowledge.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Though thou shouldst bray a fool in the mortar, as when a pestle striketh upon sodden barley, his folly would not be taken from him.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Be diligent to know the countenance of thy cattle, and consider thy own flocks:
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
For thou shalt not always have power: but a crown shall be given to generation and generation.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
The meadows are open, and the green herbs have appeared, and the hay is gathered out of the mountains.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Lambs are for thy clothing: and kids for the price of the field.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
Let the milk of the goats be enough for thy food, and for the necessities of thy house, and for maintenance for thy handmaids.

< Miyambo 27 >