< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Boast not thyself of tomorrow, for thou know not what a day may bring forth.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Let another man praise thee, and not thine own mouth, a stranger, and not thine own lips.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
A stone is heavy, and the sand weighty, but a fool's vexation is heavier than both.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Wrath is cruel, and anger is overwhelming, but who is able to stand before jealousy?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Better is open rebuke than love that is hidden.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Faithful are the wounds of a friend, but the kisses of an enemy are profuse.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
The full soul loathes a honeycomb, but to the hungry soul every bitter thing is sweet.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
As a bird that wanders from her nest, so is a man who wanders from his place.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Oil and perfume rejoice the heart, so too the sweetness of a man's friend by hearty counsel.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Forsake not thine own friend, and thy father's friend. And go not to thy brother's house in the day of thy calamity. Better is a neighbor nearby than a brother far off.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
My son, be wise, and make my heart glad, that I may answer him who reproaches me.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
A prudent man sees the evil, and hides himself. The simple pass on, and suffer for it.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Take his garment who is surety for a stranger, and hold him in pledge who is surety for a strange woman.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
He who blesses his friend with a loud voice, rising early in the morning, it shall be considered a curse to him.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
A continual dropping in a very rainy day, and a contentious woman are alike.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
He who would restrain her restrains the wind, and his right hand encounters oil.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Iron sharpens iron, so a man sharpens the countenance of his friend.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
He who keeps the fig tree shall eat the fruit of it, and he who regards his master shall be honored.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
As in water face is to face, so the heart of a man is to a man.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Sheol and Abaddon are never satisfied, and the eyes of man are never satisfied. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
The refining pot is for silver, and the furnace for gold, and a man is tried by his praise.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Though thou should pound a fool in a mortar with a pestle along with crushed grain, yet his foolishness will not depart from him.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Be thou diligent to know the state of thy flocks, and look well to thy herds.
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
For riches are not forever. And does the crown endure to all generations?
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
The hay is carried, and the tender grass shows itself, and the herbs of the mountains are gathered in.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
The lambs are for thy clothing, and the goats are the cost of the field.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
And then will be goats' milk enough for thy food; for the food of thy household, and maintenance for thy maidens.

< Miyambo 27 >