< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ros dig ikke af Dagen i Morgen, du ved jo ikke, hvad Dag kan bringe.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Lad en anden rose dig, ikke din Mund, en fremmed, ikke dine egne Læber.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Sten er tung, og Sand vejer til, men tung fremfor begge er Daarers Galde.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Vrede er grum, og Harme skummer, men Skinsyge, hvo kan staa for den?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Hellere aabenlys Revselse end Kærlighed, der skjules.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Vennehaands Hug er ærligt mente, Avindsmands Kys er mange.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Den mætte vrager Honning, alt beskt er sødt for den sultne.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Som Fugl, der maa fly fra sin Rede, er Mand, der maa fly fra sit Hjem:
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Olie og Røgelse fryder Sindet, men Sjælen sønderslides af Kummer.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Slip ikke din Ven og din Faders Ven, gaa ej til din Broders Hus paa din Ulykkes Dag. Bedre er Nabo ved Haanden end Broder i det fjerne.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Vær viis, min Søn, og glæd mit Hjerte, at jeg kan svare den, der smæder mig.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
Den kloge ser Faren og søger i Skjul, tankeløse gaar videre og bøder,
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Tag hans Klæder, han borged for en anden, pant ham for fremmedes Skyld!
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Den, som aarle højlydt velsigner sin Næste, han faar det regnet for Banden.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Ustandseligt Tagdryp en Regnvejrsdag og trættekær Kvinde ligner hinanden;
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
den, som vil skjule hende, skjuler Vind, og hans højre griber i Olie.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Jern skærpes med Jern, det ene Menneske skærper det andet.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Røgter man et Figentræ, spiser man dets Frugt; den, der vogter sin Herre, æres.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Som i Vandspejlet Ansigt møder Ansigt, slaar Menneskehjerte Menneske i Møde.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Dødsrige og Afgrund kan ikke mættes, ej heller kan Menneskens Øjne mættes. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
Digel til Sølv og Ovn til Guld, efter sit Ry bedømmes en Mand.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Om du knuste en Daare i Morter med Støder midt imellem Gryn, hans Daarskab veg dog ej fra ham.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Mærk dig, hvorledes dit Smaakvæg ser ud, hav Omhu for dine Hjorde;
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
thi Velstand varer ej evigt, Rigdom ikke fra Slægt til Slægt;
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
er Sommergræsset svundet, Grønt spiret frem, og sankes Bjergenes Urter,
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
da har du Lam til at give dig Klæder og Bukke til at købe en Mark,
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
Gedemælk til Mad for dig og dit Hus, til Livets Ophold for dine Piger.

< Miyambo 27 >