< Miyambo 27 >

1 Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
Nechlub se dnem zítřejším, nebo nevíš, coť ten den přinese.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
Nechať tě chválí jiní, a ne ústa tvá, cizí, a ne rtové tvoji.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
Tíž má kamen, a váhu písek, ale hněv blázna těžší jest nad to obé.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Ukrutnátě věc hněv a prudká prchlivost, ale kdo ostojí před závistí?
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
Lepší jest domlouvání zjevné, než milování tajné.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
Bezpečnější rány od přítele, než lahodná líbání nenávidícího.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
Duše sytá pohrdá i medem, ale duši lačné každá hořkost sladká.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
Jako pták zaletuje od hnízda svého, tak muž odchází od místa svého.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
Mast a kadění obveseluje srdce; tak sladkost přítele víc než rada vlastní.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
Přítele svého a přítele otce svého neopouštěj, a do domu bratra svého nechoď v čas bídy své; lepšíť jest soused blízký, než bratr daleký.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
Buď moudrý, synu můj, a obvesel srdce mé, ať mám co odpovědíti tomu, kdož mi utrhá.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
Opatrný vida zlé, vyhne se, ale hloupí předce jdouce, těžkosti docházejí.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
Vezmi roucho toho, kterýž slíbil za cizího, a od toho, kdo za cizozemku slíbil, základ jeho.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Tomu, kdož dobrořečí příteli svému hlasem velikým, ráno vstávaje, za zlořečení počteno bude.
15 Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
Kapání ustavičné v čas přívalu, a žena svárlivá rovní jsou sobě;
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Kdož ji schovává, schovává vítr, a jako mast v pravici voněti bude.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
Železo železem se ostří; tak muž zostřuje tvář přítele svého.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
Kdo ostříhá fíku, jídá ovoce jeho; tak kdo ostříhá pána svého, poctěn bude.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
Jakož u vodě tvář proti tváři se ukazuje, tak srdce člověka člověku.
20 Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
Propast a zahynutí nebývají nasyceni, tak oči člověka nasytiti se nemohou. (Sheol h7585)
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
Teglík stříbra a pec zlata zkušuje, tak člověka pověst chvály jeho.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
Bys blázna i v stupě mezi krupami píchem zopíchal, neodejde od něho bláznovství jeho.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
Pilně přihlídej k dobytku svému, pečuj o stáda svá.
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Nebo ne na věky trvá bohatství, ani koruna do pronárodu.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
Když zroste tráva, a ukazuje se bylina, tehdáž ať se shromažďuje seno s hor.
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
Beránkové budou k oděvu tvému, a záplata pole kozelci.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
Nadto dostatek mléka kozího ku pokrmu tvému, ku pokrmu domu tvého, a živnosti děvek tvých.

< Miyambo 27 >