< Miyambo 26 >

1 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
Кум ну се потривеск зэпада вара ши плоая ын тимпул сечеришулуй, аша ну се потривеште слава пентру ун небун.
2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
Кум саре врабия ынкоаче ши ынколо ши кум збоарэ рындуника, аша ну нимереште блестемул неынтемеят.
3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
Бичул есте пентру кал, фрыул, пентру мэгар ши нуяуа, пентру спинаря небунилор.
4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
Ну рэспунде небунулуй дупэ небуния луй, ка сэ ну семень ши ту ку ел.
5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
Рэспунде ынсэ небунулуй дупэ небуния луй, ка сэ ну се крядэ ынцелепт.
6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
Чел че тримите о солие принтр-ун небун ышь тае сингур пичоареле ши бя недрептатя.
7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
Кум сунт пичоареле ологулуй, аша есте ши о ворбэ ынцеляптэ ын гура унор небунь.
8 Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
Кум ай пуне о пятрэ ын праштие, аша есте кынд дай мэрире унуй небун.
9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
Ка ун спин каре вине ын мына унуй ом бят, аша есте о ворбэ ынцеляптэ ын гура небунилор.
10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
Ка ун аркаш каре рэнеште пе тоатэ лумя, аша есте чел че токмеште пе небунь ши пе ынтыий вениць.
11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
Кум се ынтоарче кынеле ла че а вэрсат, аша се ынтоарче небунул ла небуния луй.
12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
Дакэ везь ун ом каре се креде ынцелепт, поць сэ ай май мултэ нэдежде пентру ун небун декыт пентру ел.
13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
Ленешул зиче: „Афарэ есте ун леу, пе улице есте ун леу!”
14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
Кум се ынвыртеште уша пе цыцыниле ей, аша се ынвыртеште ленешул ын патул луй.
15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
Ленешул ышь вырэ мына ын блид ши-й вине греу с-о дукэ ярэшь ла гурэ.
16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
Ленешул се креде май ынцелепт декыт шапте оамень каре рэспунд ку жудекатэ.
17 Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
Ун трекэтор каре се аместекэ ынтр-о чартэ каре ну-л привеште есте ка унул каре апукэ ун кыне де урекь.
18 Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
Ка небунул каре арункэ сэӂець апринсе ши учигэтоаре,
19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
аша есте омул каре ыншалэ пе апроапеле сэу ши апой зиче: „Ам врут доар сэ глумеск!”
20 Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
Кынд ну май сунт лемне, фокул се стинӂе; ши кынд ну май есте ничун клеветитор, чарта се потолеште.
21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
Дупэ кум кэрбунеле фаче жэратик ши лемнул, фок, тот аша ши омул гылчевитор апринде чарта.
22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
Кувинтеле клеветиторулуй сунт ка ниште прэжитурь, алунекэ пынэ ын фундул мэрунтаелор.
23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
Ка згура де арӂинт пусэ пе ун чоб де пэмынт, аша сунт бузеле апринсе ши о инимэ ря.
24 Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
Чел че урэште се префаче ку бузеле луй ши ынэунтрул луй прегэтеште ыншелэчуня.
25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
Кынд ыць ворбеште ку глас дулче, ну-л креде, кэч шапте урычунь сунт ын инима луй.
26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
Кяр дакэ-шь аскунде ура ын префэкэторие, тотушь рэутатя луй се ва дескопери ын адунаре.
27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
Чине сапэ гроапа алтуя каде ел ын еа ши пятра се ынтоарче песте чел че о прэвэлеште.
28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
Лимба минчиноасэ урэште пе чей пе каре-й добоарэ еа ши гура лингушитоаре прегэтеште пеиря.

< Miyambo 26 >