< Miyambo 26 >

1 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
چنانکه برف در تابستان و باران درحصاد، همچنین حرمت برای احمق شایسته نیست.۱
2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
لعنت، بی‌سبب نمی آید، چنانکه گنجشک در طیران و پرستوک در پریدن.۲
3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
شلاق به جهت اسب و لگام برای الاغ، وچوب از برای پشت احمقان است.۳
4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
احمق را موافق حماقتش جواب مده، مباداتو نیز مانند او بشوی.۴
5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
احمق را موافق حماقتش جواب بده، مباداخویشتن را حکیم بشمارد.۵
6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
هر‌که پیغامی به‌دست احمق بفرستد، پایهای خود را می‌برد و ضرر خود را می‌نوشد.۶
7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
ساقهای شخص لنگ بی‌تمکین است، ومثلی که از دهان احمق برآید همچنان است.۷
8 Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
هر‌که احمق را حرمت کند، مثل کیسه جواهر در توده سنگها است.۸
9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
مثلی که از دهان احمق برآید، مثل خاری است که در دست شخص مست رفته باشد.۹
10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
تیرانداز همه را مجروح می‌کند، همچنان است هر‌که احمق را به مزد گیرد و خطاکاران رااجیر نماید.۱۰
11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
چنانکه سگ به قی خود برمی گردد، همچنان احمق حماقت خود را تکرار می‌کند.۱۱
12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
آیا شخصی را می‌بینی که در نظر خودحکیم است، امید داشتن بر احمق از امید بر اوبیشتر است.۱۲
13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
کاهل می‌گوید که شیر در راه است، و اسددر میان کوچه‌ها است.۱۳
14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
چنانکه در بر پاشنه‌اش می‌گردد، همچنان کاهل بر بستر خویش.۱۴
15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
کاهل دست خود را در قاب فرو می‌برد و ازبرآوردن آن به دهانش خسته می‌شود.۱۵
16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
کاهل در نظر خود حکیمتر است از هفت مرد که جواب عاقلانه می‌دهند.۱۶
17 Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
کسی‌که برود و در نزاعی که به او تعلق ندارد متعرض شود، مثل کسی است که گوشهای سگ را بگیرد.۱۷
18 Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
آدم دیوانه‌ای که مشعلها و تیرها و موت رامی اندازد،۱۸
19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
مثل کسی است که همسایه خود را فریب دهد، و می‌گوید آیا شوخی نمی کردم؟۱۹
20 Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
از نبودن هیزم آتش خاموش می‌شود، و ازنبودن نمام منازعه ساکت می‌گردد.۲۰
21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
زغال برای اخگرها و هیزم برای آتش است، و مرد فتنه انگیز به جهت برانگیختن نزاع.۲۱
22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
سخنان نمام مثل خوراک لذیذ است، که به عمقهای دل فرو می‌رود.۲۲
23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
لبهای پرمحبت با دل شریر، مثل نقره‌ای پردرد است که بر ظرف سفالین اندوده شود.۲۳
24 Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
هر‌که بغض دارد با لبهای خود نیرنگ می‌نماید، و در دل خود فریب را ذخیره می‌کند.۲۴
25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
هنگامی که سخن نیکو گوید، او را باور مکن زیرا که در قلبش هفت چیز مکروه است.۲۵
26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
هر‌چند بغض او به حیله مخفی شود، اماخباثت او در میان جماعت ظاهر خواهد گشت.۲۶
27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
هر‌که حفره‌ای بکند در آن خواهد افتاد، وهر‌که سنگی بغلطاند بر او خواهد برگشت.۲۷
28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
زبان دروغگو از مجروح شدگان خود نفرت دارد، و دهان چاپلوس هلاکت را ایجاد می‌کند.۲۸

< Miyambo 26 >