< Miyambo 26 >

1 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
Som Sneen om Sommeren og som Regnen om Høsten saa passer Ære ikke for en Daare.
2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
Som en Spurv i Fart, som en Svale i Flugt saaledes vil en Forbandelse, som sker uden Aarsag, ikke træffe ind.
3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
En Svøbe er for Hesten og en Tømme for Asenet og et Ris for Daarers Ryg.
4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
Svar ej en Daare efter hans Taabelighed, at ikke ogsaa du skal blive ham lig.
5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
Svar en Daare efter hans Taabelighed, at han ikke skal være viis i sine egne Øjne.
6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
Fødderne hugger den af sig, og Fortrædelighed maa den drikke, som sender Bud ved en Daare.
7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
Tager Benene fra den halte og Tankesproget bort, som er i Daarers Mund.
8 Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
Som den, der binder Stenen fast i Slyngen, saa er den, der giver en Daare Ære.
9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
Som en Tjørnekæp, der kommer i den druknes Haand, saa er Tankesproget i Daarers Mund.
10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
Som en Pil, der saarer alt, saa er den, der lejer en Daare, og den, der lejer vejfarende.
11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
Ligesom en Hund vender sig til sit eget Spy, saa er Daaren, som gentager sin Taabelighed.
12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
Har du set en Mand, som er viis i sine egne Øjne, da er der mere Forhaabning om en Daare end om ham.
13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
Den lade siger: Der er en grum Løve paa Vejen, en Løve paa Gaderne.
14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
Som Døren drejer sig om paa sine Hængsler, saa den lade paa sin Seng.
15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
Den lade stikker sin Haand i Fadet; det bliver ham besværligt at lade den komme til sin Mund igen.
16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
Den lade er visere i sine egne Øjne end syv, som svare forstandigt.
17 Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
Som den, der griber Hunden fat ved Ørene, saa er den, der gaar forbi og kommer i Vrede over en Trætte, der ikke kommer ham ved.
18 Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
Som en gal, der udkaster Gnister, Pile og Død,
19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
saa er den Mand, der besviger sin Næste og siger: Skæmter jeg ikke?
20 Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
Naar der intet Ved er mere, udslukkes Ilden; og naar der ingen Bagvadsker er, stilles Trætte.
21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
Kul til Gløder og Ved til Ild: Saa er en trættekær Mand til at optænde Kiv.
22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
En Bagvadskers Ord lyde som Skæmt, dog trænge de ind i inderste Bug.
23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
Som et Potteskaar, der er overdraget med urent Sølv, saa ere brændende Læber og et ondt Hjerte.
24 Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
Den hadefulde forstiller sig med sine Læber, men inden i sig nærer han Svig.
25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
Naar han gør sin Røst yndig, da tro ham ikke; thi der er syv Vederstyggeligheder i hans Hjerte.
26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
Den, hvis Had er skjult ved Bedrag, hans Ondskab skal blive aabenbaret i Forsamlingen.
27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
Hvo som graver en Grav, skal selv falde i den; og hvo som vælter en Sten op, paa ham skal den falde tilbage.
28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
En falsk Tunge hader dem, som den har knust, og en glat Mund bereder Fald.

< Miyambo 26 >