< Miyambo 25 >

1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
Eyinom yɛ Salomo mmebusɛm nkekaho a Yudahene Hesekia afotufo kyerɛwee:
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
Ɛyɛ Onyankopɔn anuonyamhyɛ sɛ wɔde asɛm sie; sɛ wɔpɛɛpɛɛ asɛm mu nso hyɛ ahemfo anuonyam.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Sɛnea ɔsoro korɔn na asase mu dɔ no, saa ara na wɔrentumi nhwehwɛ ahemfo koma mu.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Sɛ woyi dwetɛ ho fi a, na ato nea ɛkɔ dwetɛdwumfo nsam;
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Yi amumɔyɛfo fi ɔhene anim, na trenee bɛma nʼahengua atim.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Mma wo ho so wɔ ɔhene anim, na mpere dibea wɔ atitiriw mu;
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
Eye ma no sɛ ɔbɛka akyerɛ wo se, “Bra soro ha,” sen sɛ ɔbɛbrɛ wo ase wɔ otitiriw bi anim. Nea wode wʼani ahu no
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
mpɛ ntɛm mfa nkɔ asennii, na sɛ awiei no wo yɔnko gu wʼanim ase a dɛn na wobɛyɛ?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Sɛ wo ne wo yɔnko di asɛm a nna obi foforo ahintasɛm adi,
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
anyɛ saa a, nea ɔbɛte no begu wʼanim ase na din bɔne a wubenya no rempepa da.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Asɛm a wɔka no sɛnea ɛfata no te sɛ sika kɔkɔɔ a wɔabɔ sɛ aprɛ de atuatua dwetɛ nsiesiei mu.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Sikakɔkɔɔ asokaa anaa sikakɔkɔɔ ankasa ahyehyɛde te sɛ onyansafo animka a ɔde ma nea ɔyɛ aso ma no.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Sɛnea sukyerɛmma ma wim dwo wɔ otwabere mu no, saa ara na ɔsomafo nokwafo te ma wɔn a wɔsoma no no; na ɔma ne wuranom akomatɔyam.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Omununkum ne mframa a ɛmfa osu mma no te sɛ onipa a ɔde akyɛde a ɔmmfa mma hoahoa ne ho.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Ntoboase ma sodifo ti da, na tɛkrɛmabere tumi bu dompe mu.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Sɛ wunya ɛwo a, nni ntra so, ne bebrebe bɛma woafe.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Ntaa nkɔ wo yɔnko fi, wo ho fono no a, ɔbɛtan wo.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Onipa a odi adansekurum tia ne yɔnko no te sɛ kontibaa, afoa anaa bɛmma a ano yɛ nnam.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Ɛse a ɛyare ɔkekaw anaa nan a ɛyɛ apakye te sɛ nea wode wo ho to ɔtorofo so hiada mu.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
Nea ɔto dwom kyerɛ ɔwerɛhowni no, te sɛ nea ɔpa ntama gu awɔwbere mu anaa te sɛ nsa nyinyanyinya a wohwie gu apirakuru so.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
Sɛ ɔkɔm de wo tamfo a, ma no aduan nni; sɛ osukɔm de no a, ma no nsu nnom.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
Sɛ woyɛ saa a, wobɛsosɔ nnyansramma agu nʼatifi, na Awurade bɛma wo akatua.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
Sɛnea atifi fam mframa de osu ba no, saa ara na tɛkrɛma a edi nseku de omuna ba.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
Eye sɛ wobɛtena suhyɛ twɔtwɔw ase baabi, sen sɛ wo ne ɔyere tɔkwapɛfo bɛtena fie.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Nsuonwini a ɔkra a atɔ beraw nya no te sɛ anigyesɛm a efi akyirikyiri.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Asuti a afono anaa abura a ayɛ pɔtɔɔ te sɛ ɔtreneeni a ogyaa ne ho ma amumɔyɛfo.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
Enye sɛ wodi ɛwo ntraso, saa ara na ɛnyɛ anuonyam sɛ obi bɛhwehwɛ nsɛm a mu dɔ mu.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Onipa a onni ahohyɛso no te sɛ kuropɔn a nʼafasu abubu agu fam.

< Miyambo 25 >