< Miyambo 25 >
1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
Aquí hay más proverbios de Salomón, recopilados por los escribas de Ezequías, rey de Judá.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
La grandeza de Dios está en las cosas ocultas, mientras que la grandeza de los reyes está en revelar lo desconocido.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Así como la altura de los cielos y la profundidad de la tierra, el pensamiento de un rey no se puede conocer.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Quita la escoria de la plata y el platero tendrá plata pura para hacer su trabajo.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Quita al malvado de la presencia del rey, y el rey gobernará confiado y con justicia.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
No trates de parecer grande delante del rey, y no finjas para estar entre la gente importante.
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
Porque es mejor que te digan: “Ven aquí arriba”, que ser humillado delante de un noble. Aunque hayas visto algo con tus propios ojos,
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
no corras a tomar acciones legales, porque ¿qué harás al final cuando tu vecino demuestre que estás equivocado y te humille?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Debate el caso primero con tu vecino, y no traiciones el secreto que otra persona te ha confiado,
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
de lo contrario el que escuche te avergonzará y no podrás recuperarte de tu mala reputación.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
El consejo impartido en el momento correcto es como manzanas de oro con baño de plata.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
La crítica constructiva de los sabios a quien escucha el consejo, es como un anillo de oro y un collar de oro fino.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
El mensajero fiel es un fresco para su maestro, como la nieve fresca en un día caluroso de siega.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Quien se jacta de un regalo que nunca entrega, es como las nubes y el viento sin lluvia.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Si eres paciente, podrás persuadir a tu superior, y las palabras suaves pueden derribar la oposición.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Si hallas dinero, come lo necesario; porque si comes demasiado, te enfermarás.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
No visites la casa de tu vecino con mucha frecuencia, o se cansarán y te aborrecerán.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Mentir en la corte contra un amigo es como atacarlo con una maza, con una espada o con una lanza.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Confiar en las personas poco fiables en momentos de dificultad es como comer con un diente partido, o caminar con un pie herido.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
Cantar canciones alegres a quien tiene el corazón quebrantado, es como quitarte el abrigo en un día de frio, o poner vinagre en una herida abierta.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
Si tu enemigo tiene hambre, dale de comer; si tiene sed, dale de beber.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
Esto hará que se avergüence como si tuviera carbones encendidos sobre su cabeza, y el Señor te recompensara.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
Así como el viento del norte trae la lluvia, las personas calumniadoras hacen enojar.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
Mejor es vivir en un rincón de la azotea, que compartir toda la casa con una mujer conflictiva.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Las buenas noticias que vienen de un país lejano son como agua fresca para un viajero cansado.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Los justos que ceden ante los malvados son como una fuente llena de barro, o un pozo contaminado.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
No es bueno comer mucha miel, tampoco desear mucha alabanza.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Una persona sin dominio propio es como una ciudad expuesta, cuyos muros están agrietados.