< Miyambo 25 >

1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
Tambem estes são proverbios de Salomão, os quaes transcreveram os homens d'Ezequias, rei de Judah.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
A gloria de Deus é encobrir o negocio; mas a gloria dos reis esquadrinhar o negocio.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Para a altura dos céus, e para a profundeza da terra, e para o coração dos reis, não ha investigação.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Tira da prata as escorias, e sairá vaso para o fundidor.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Tira o impio da presença do rei, e o seu throno se affirmará na justiça.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Não te glories na presença do rei, nem te ponhas no logar dos grandes;
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
Porque melhor é que te digam: Sobe aqui; do que seres humilhado diante do principe que já viram os teus olhos.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
Não saias depressa a litigar, para que depois ao fim não saibas que fazer, podendo-te confundir o teu proximo.
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Pleiteia o teu pleito com o teu proximo, e não descubras o segredo d'ontro:
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
Para que não te deshonre o que o ouvir, e a tua infamia se não aparte de ti.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Como maçãs d'oiro em salvas de prata, assim é a palavra dita a seu tempo.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Como pendentes d'oiro e gargantilhas d'oiro fino, assim é o sabio reprehensor para o ouvido ouvinte.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Como frieza de neve no tempo da sega, assim é o mensageiro fiel para com os que o enviam; porque recreia a alma de seu senhor.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Como nuvens e ventos que não trazem chuva, assim é o homem que se gaba falsamente de dadivas.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Pela longanimidade se persuade o principe, e a lingua branda quebranta os ossos.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Achaste mel? come o que te basta; para que porventura não te fartes d'elle, e o venhas a vomitar.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Retira o teu pé da casa do teu proximo; para que se não enfade de ti, e te aborreça.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Martello, e espada, e frecha aguda é o homem que diz falso testemunho contra o seu proximo.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Como dente quebrado, e pé desengonçado, é a confiança no desleal, no tempo da angustia.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
O que canta canções ao coração afflicto é como aquelle que despe o vestido n'um dia de frio, e como vinagre sobre salitre.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
Se o que te aborrece tiver fome, dá-lhe pão para comer; e se tiver sêde, dá-lhe agua para beber;
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
Porque assim brazas lhe amontoarás sobre a cabeça; e o Senhor t'o pagará.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
O vento norte afugenta a chuva, e a face irada a lingua fingida.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
Melhor é morar n'um canto do terraço, do que com a mulher contenciosa, e isso em casa em que mais companhia haja.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Como agua fria á alma cançada, taes são as boas novas de terra remota.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Como fonte turva, e manancial corrupto, assim é o justo que cae diante do impio.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
Comer muito mel não é bom; assim a pesquiza da propria gloria não é gloria.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Como a cidade derribada, sem muro, assim é o homem que não pode conter o seu espirito.

< Miyambo 25 >