< Miyambo 25 >

1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
These also are proverbs of Solomon, which the men of Hezekiah king of Judah copied out.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
It is the glory of God to conceal a thing, but the glory of kings is to search out a matter.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
As the heavens for height, and the earth for depth, so the hearts of kings are unsearchable.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Take away the dross from the silver, and material comes out for the refiner;
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Take away the wicked from the king's presence, and his throne will be established in righteousness.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Do not exalt yourself in the presence of the king, or claim a place among great men;
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
for it is better that it be said to you, "Come up here," than that you should be put lower in the presence of the prince, whom your eyes have seen.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
Do not be hasty in bringing charges to court. What will you do in the end when your neighbor shames you?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Debate your case with your neighbor, and do not betray the confidence of another;
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
lest one who hears it put you to shame, and your bad reputation never depart.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
A word fitly spoken is like apples of gold in settings of silver.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
As an earring of gold, and an ornament of fine gold, so is a wise reprover to an obedient ear.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
As the cold of snow in the time of harvest, so is a faithful messenger to those who send him; for he refreshes the soul of his masters.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
As clouds and wind without rain, so is he who boasts of gifts deceptively.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
By patience a ruler is persuaded. A soft tongue breaks the bone.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Have you found honey? Eat as much as is sufficient for you, lest you eat too much, and vomit it.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Let your foot be seldom in your neighbor's house, lest he be weary of you, and hate you.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
A man who gives false testimony against his neighbor is like a club, a sword, or a sharp arrow.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Confidence in someone unfaithful in time of trouble is like a bad tooth, or a lame foot.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
As one who takes away a garment in cold weather, or vinegar on soda, so is one who sings songs to a heavy heart.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
If your enemy is hungry, give him something to eat. If he is thirsty, give him something to drink,
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
for by doing this you will heap coals of fire on his head, and the LORD will reward you.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
The north wind brings forth rain: so a backbiting tongue brings an angry face.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
It is better to dwell in the corner of the housetop, than to share a house with a contentious woman.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Like cold water to a thirsty soul, so is good news from a far country.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Like a muddied spring, and a polluted well, so is a righteous man who gives way before the wicked.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
It is not good to eat much honey; nor is it honorable to seek one's own honor.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Like a city that is broken down and without walls is a man whose spirit is without restraint.

< Miyambo 25 >