< Miyambo 25 >
1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
These are also parables of Solomon, which the men of Ezechias king of Juda copied out.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
It is the glory of God to conceal the word, and the glory of kings to search out the speech.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
The heaven above, and the earth beneath, and the heart of kings is unsearchable.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Take away the rust from silver, and there shall come forth a most pure vessel:
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Take away wickedness from the face of the king, and his throne shall be established with justice.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Appear not glorious before the king, and stand not in the place of great men.
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
For it is better that it should be said to thee: Come up hither; than that thou shouldst be humbled before the prince.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
The things which thy eyes have seen, utter not hastily in a quarrel: lest afterward thou mayst not be able to make amends, when thou hast dishonoured thy friend.
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Treat thy cause with thy friend, and discover not the secret to a stranger:
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
Lest he insult over thee, when he hath heard it, and cease not to upbraid thee. Grace and friendship deliver a man: keep these for thyself, lest thou fall under reproach.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
To speak a word in due time, is like apples of gold on beds of silver.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
As an earring of gold and a bright pearl, so is he that reproveth the wise, and the obedient ear.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
As the cold of snow in the time of harvest, so is a faithful messenger to him that sent him, for he refresheth his soul.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
As clouds, and wind, when no rain followeth, so is the man that boasteth, and doth not fulfill his promises.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
By patience a prince shall be appeased, and a soft tongue shall break hardness.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Thou hast found honey, eat what is sufficient for thee, lest being glutted therewith thou vomit it up.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Withdraw thy foot from the house of thy neighbour, lest having his fill he hate thee.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
A man that beareth false witness against his neighbour, is like a dart and a sword and a sharp arrow.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
To trust to an unfaithful man in the time of trouble, is like a rotten tooth, and weary foot,
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
And one that looseth his garment in cold weather. As vinegar upon nitre, so is he that singeth songs to a very evil heart. As a moth doth by a garment, and a worm by the wood: so the sadness of a man consumeth the heart.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
If thy enemy be hungry, give him to eat: if he thirst, give him water to drink:
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
For thou shalt heap hot coals upon his head, and the Lord will reward thee.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
The north wind driveth away rain, as doth a sad countenance a backbiting tongue.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
It is better to sit in a corner of the housetop, than with a brawling woman, and in a common house.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
As cold water to a thirsty soul, so is good tidings from a far country.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
A just man falling down before the wicked, is as a fountain troubled with the foot, and a corrupted spring.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
As it is not good for a man to eat much honey, so he that is a searcher of majesty, shall be overwhelmed by glory.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
As a city that lieth open and is not compassed with walls, so is a man that cannot refrain his own spirit in speaking.