< Miyambo 25 >
1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
Disse ere ogsaa Salomos Ordsprog, hvilke Judas Konge, Ezekias's Mænd have samlet.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
Det er Guds Ære at skjule en Ting, men det er Kongers Ære at ransage en Ting.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Himmelen i Højhed og Jorden i Dybde og Kongers Hjerte ere uransagelige.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Man borttog Slaggerne fra Sølvet, saa fik Guldsmeden et Kar ud deraf;
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
man borttage den ugudelige, som er for Kongens Ansigt, saa skal hans Trone befæstes ved Retfærdighed.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Bram ikke for Kongens Ansigt, og stil dig ikke paa de mægtiges Sted!
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
Thi det er bedre, at man siger til dig: Stig her op! end at man skal sætte dig ned for en Fyrstes Ansigt, som dine Øjne have set.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
Gak ikke hastelig ud for at trætte, at du ikke skal begaa noget som helst paa det sidste, naar din Næste har beskæmmet dig.
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Før din Sag imod din Næste; men aabenbar ikke en andens Hemmelighed,
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
paa det den, som det hører, ikke skal forhaane dig, og dit onde Rygte ikke vige fra dig.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Som Guldæbler i Sølvskaaler af udgravet Arbejde er det Ord, som tales i rette Tid.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Som et gyldent Smykke og en kostbar Prydelse vil den, som irettesætter viselig, være for det Øre, som hører efter.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Som Sneens Kølighed paa en Høstdag er et trofast Bud for dem, som sende ham, og han vederkvæger sine Herrers Sjæl.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Som Taage og Vejr uden Regn er den Mand, som praler med at ville give, men skuffer.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Ved Langmodighed overtales en Fyrste, og en blød. Tunge sønderbryder Ben.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Har du fundet Honning, saa spis til din Nødtørft, at du ej skal mættes af den og udspy den.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Lad din Fod sjælden komme i din Vens Hus, at han ej skal blive ked af dig og hade dig.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Som en Hammer og et Sværd og en hvas Pil er den Mand, som siger falsk Vidnesbyrd imod sin Næste.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Som en skør Tand og en Fod, der snubler, er Tillid til den troløse paa Nødens Dag.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
Som den, der aflægger Klæderne den Dag, det er koldt, som Eddike paa Salpeter, saa er den, som synger Sange for et bedrøvet Hjerte.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
Dersom din Fjende hungrer, giv ham Brød at æde; og dersom han tørster, giv ham Vand at drikke;
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
thi du skal samle Gløder paa hans Hoved, og Herren skal betale dig det.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
Nordenvejret føder Regn og den Tunge, som taler i Skjul, et vredt Ansigt.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
Det er bedre at bo i Hjørnet paa et Tag end hos en trættekær Kvinde og i Hus sammen.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Som koldt Vand for en træt Sjæl, saa er et godt Budskab fra et langt fraliggende Land.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Som en plumret Kilde og en fordærvet Brønd er den retfærdige, som snubler for en ugudelig.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
At æde megen Honning er ikke godt; ej heller er det en Ære, naar Folk ransage deres egen Ære.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Som en gennembrudt Stad uden Mur, saa er en Mand, som ikke kan tvinge sin Aand.