< Miyambo 25 >

1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
I ovo su mudre izreke Salomonove; sabrali ih ljudi Ezekije, kralja judejskog.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
Slava je Božja sakrivati stvar, a slava kraljevska istraživati je.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Neistražljivo je nebo u visinu, zemlja u dubinu i srce kraljevsko.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Ukloni trosku od srebra, i uspjet će posao zlataru.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Ukloni opakoga ispred kralja, i utvrdit će se pravicom prijestol njegov.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Ne veličaj se pred kraljem i ne sjedaj na mjesto velikaško,
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
jer je bolje da ti se kaže: “Popni se gore” nego da te ponize pred odličnikom.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
Što su ti oči vidjele ne iznosi prebrzo na raspru; jer što ćeš učiniti na koncu kad te opovrgne bližnji tvoj?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Kad si u parbi s bližnjim svojim, ne otkrivaj tuđe tajne,
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
da te ne izgrdi tko čuje i da ti se kleveta ne vrati.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Riječi kazane u pravo vrijeme zlatne su jabuke u srebrnim posudama.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Mudrac koji kori uhu je poslušnu zlatan prsten i ogrlica od tanka zlata.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Vjeran je glasnik onomu tko ga šalje kao ledena studen u doba žetve: on krijepi dušu svoga gospodara.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Tko se diči lažljivim darom, on je kao oblak i vjetar bez kiše.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Strpljivošću se ublažava sudac, mek jezik i kosti lomi.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Kad naiđeš na med, jedi umjereno, kako se ne bi prejeo i pojedeno izbljuvao.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Rijetko zalazi u kuću bližnjega svoga, da te se ne zasiti i ne zamrzi na te.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Čovjek koji svjedoči lažno na bližnjega svoga on je kao bojni malj i mač i oštra strijela.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Uzdanje u bezbožnika na dan nevolje - krnjav je zub i noga klecava.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
Kao onaj koji skida haljinu u zimski dan ili ocat lije na ranu, takav je onaj tko pjeva pjesmu turobnu srcu.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
Ako je gladan neprijatelj tvoj, nahrani ga kruhom, i ako je žedan, napoji ga vodom.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
Jer mu zgrćeš ugljevlje na glavu i Jahve će ti platiti.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
Sjeverni vjetar donosi dažd, a himben jezik srdito lice.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
Bolje je stanovati pod rubom krova nego u zajedničkoj kući sa ženom svadljivom.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Kao studena voda žednu grlu, takva je dobra vijest iz zemlje daleke.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
Kao zatrpan izvor i vrelo zamućeno, takav je pravednik koji kleca pred opakim.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
Jesti mnogo meda nije dobro niti tražiti pretjerane časti.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Grad razvaljen i bez zidova - takav je čovjek koji nema vlasti nad sobom.

< Miyambo 25 >