< Miyambo 24 >
1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Mma wʼani mmere amumɔyɛfo, mfa wo ho mmɔ wɔn;
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
Efisɛ wɔn koma dwene atirimɔdensɛm ho, na wɔn ano ka nea ɛde basabasayɛ ba ho asɛm.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Wɔde nyansa na esi fi, na nhumu mu na wɔma etim;
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
ɛnam nimdeɛ so na wonya ademude a ɛho yɛ na na ɛyɛ fɛ hyehyɛ nʼadan mu.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Onyansafo wɔ tumi a ɛso, na onimdefo nyin ahoɔden mu;
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
nea ɔretu sa hia akwankyerɛ, nea ɔrehwehwɛ nkonimdi no hia afotufo pii.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Nyansa wɔ soro dodo ma ɔkwasea; wɔ apon ano aguabɔ mu no, ɛnsɛ sɛ wobue wɔn ano.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Onipa a ɔbɔ pɔw bɔne no, wɔbɛfrɛ no ɔkɔtwebrɛfo.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Ogyimifo nhyehyɛe yɛ bɔne, nnipa kyi ɔfɛwdifo.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Sɛ wʼaba mu gow wɔ ɔhaw mu a, na wʼahoɔden sua!
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Gye wɔn a wɔde wɔn rekɔ akokum wɔn no nkwa; na sianka wɔn a wɔtɔ ntintan kɔ akumii.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Sɛ woka se, “Na yennim eyi ho hwee a,” nea ɔkari koma hwɛ no nhu ana? Nea ɔbɔ wo nkwa ho ban no nnim ana? Ɔrentua nea obiara ayɛ so ka ana?
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Me ba, di ɛwo, efisɛ eye; ɛwokyɛm mu wo yɛ wʼanom dɛ.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Hu nso sɛ nyansa yɛ wo kra dɛ; sɛ wunya a, wowɔ anidaso ma daakye, na wʼanidaso renyɛ ɔkwa.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Nkɔtɛw ɔtreneeni fi sɛ ɔkwanmukafo, na nkɔtow nhyɛ nʼatenae so,
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
Ɛwɔ mu sɛ ɔtreneeni hwe ase mpɛn ason de, nanso ɔsɔre bio, na amumɔyɛfo de amanehunu baako ma wɔhwe ase.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Sɛ wo tamfo hwe ase a mma ɛnyɛ wo dɛ; na sɛ ohintiw a mma wo koma nni ahurusi,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
efisɛ Awurade behu wʼadwene na ɔrempɛ na obeyi nʼabufuwhyew afi no so.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Nhaw wo ho wɔ abɔnefo nti, na mma wʼani mmere amumɔyɛfo nso,
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
efisɛ, ɔbɔnefo nni anidaso biara daakye, na wobedum amumɔyɛfo kanea.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Me ba, suro Awurade ne ɔhene, na mfa wo ho mmɔ atuatewfo ho,
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
efisɛ saa baanu yi de, ɔsɛe bɛba wɔn so mpofirim; na hena na onim amanehunu ko a wobetumi de aba?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
Eyinom nso yɛ anyansafo Nsɛnka: Atemmu a nhwɛanim wɔ mu no nye:
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
Obiara a ɔbɛka akyerɛ nea odi fɔ se, “Wo ho nni asɛm” no, nnipa bɛdome no na amanaman remmɔ no din pa.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
Na wɔn a wobu afɔdifo fɔ no, ebesi wɔn yiye, na nhyira bɛba wɔn so.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
Mmuae pa te sɛ mfewano.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Wie wo mfikyidwuma na siesie wo mfuw; ɛno akyi, si wo fi.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Nni adanse ntia ɔyɔnko a ɔnyɛɛ wo hwee, na mfa wʼano nnaadaa.
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Nka se, “Nea wayɛ me no me nso mɛyɛ no bi; nea ɔyɛe no mitua no so ka.”
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Menantew faa onihawfo afuw ho, twaa mu wɔ nea onni adwene bobeturo nso ho;
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
nsɔe afuw wɔ baabiara, wura afuw akata asase no so, na abo afasu no nso abubu.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Mede me koma kɔɔ nea mihuu no so na misuaa biribi fii mu:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
nna kakra, nkotɔ kakra, nsa a woabobɔw de rehome kakra
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
bɛma ohia aba wo so sɛ ɔkwanmukafo, na nneɛma ho nna bɛba wo so sɛ obi a okura akode. Na ohia bɛtow akyere wo sɛ ɔkwanmukafo; ahokyere bɛtoa wo sɛ ɔkorɔmfowerɛmfo.