< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
No tengas envidia de los hombres malos: ni desees estar con ellos.
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
Porque su corazón piensa en robar; e iniquidad hablan sus labios.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Con sabiduría se edificará la casa; y con prudencia se afirmará.
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
Y con ciencia las cámaras se henchirán de todas riquezas preciosas y hermosas.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
El hombre sabio es fuerte; y el hombre entendido es valiente de fuerza.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
Porque con industrias harás la guerra; y la salud está en la multitud de los consejeros.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Alta está para el insensato la sabiduría: en la puerta no abrirá su boca.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Al que piensa mal hacer, al tal, hombre de malos pensamientos le llamarán.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
El mal pensamiento del insensato es pecado; y abominación a los hombres el burlador.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Si fueres flojo en el día de trabajo, tu fuerza será angosta.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
¿Detenerte has de escapar los que son tomados para la muerte, y los que son llevados al degolladero?
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Si dijeres: Ciertamente no lo supimos: ¿el que pesa los corazones no lo entenderá? El que mira por tu alma él lo conocerá, el cual dará al hombre según sus obras.
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Come, hijo mío, de la miel, porque es buena; y del panal dulce a tu paladar:
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Tal será el conocimiento de la sabiduría a tu alma, si la hallares; y al fin tu esperanza no será cortada.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
O! impío, no aseches a la tienda del justo: no saquees su acostadero:
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
Porque siete veces cae el justo, y se torna a levantar: mas los impíos caerán en el mal.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Cuando cayere tu enemigo, no te huelgues; y cuando tropezare, no se alegre tu corazón:
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
Porque Jehová no lo mire, y le desagrade; y aparte de sobre él su enojo.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
No te entremetas con los malignos, ni tengas envidia de los impíos:
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
Porque para el malo no habrá buen fin; y la candela de los impíos será apagada.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Teme a Jehová, hijo mío, y al rey: no te entremetas con los inmutadores:
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
Porque su quebrantamiento se levantará de repente: ¿y el quebrantamiento de ambos quién lo comprenderá?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
También estas cosas pertenecen a los sabios. Tener respeto a personas en el juicio, no es bueno.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
El que dijere al malo, justo eres: los pueblos le maldecirán, y las naciones le detestarán:
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
Mas los que le reprenden, serán agradables; y sobre ellos vendrá bendición de bien.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
Los labios serán besados, del que responde palabras rectas.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Apareja de fuera tu obra, y dispónela en tu heredad; y después edificarás tu casa.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
No seas testigo sin causa contra tu prójimo; y no lisonjees con tus labios.
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
No digas: Como me hizo, así le haré: daré el pago al varón según su obra.
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Pasé junto a la heredad del hombre perezoso, y junto a la viña del hombre falto de entendimiento.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
Y he aquí que por toda ella habían ya crecido espinas, ortigas habían ya cubierto su superficie, y su cerca de piedra estaba ya destruida.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Y yo miré, y púse lo en mi corazón: lo ví, y recibí enseñanza.
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
Tomando un poco de sueño, cabeceando otro poco, poniendo mano sobre mano otro poco para volver a dormir:
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
Vendrá como caminante, tu necesidad; y tu pobreza como hombre de escudo.

< Miyambo 24 >