< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Ну пизмуи пе оамений чей рэй ши ну дори сэ фий ку ей;
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
кэч инима лор се гындеште ла прэпэд ши бузеле лор ворбеск нелеӂюирь.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Прин ынцелепчуне се ыналцэ о касэ ши прин причепере се ынтэреште;
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
прин штиинцэ се умплу кэмэриле ей де тоате бунэтэциле де прец ши плэкуте.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Ун ом ынцелепт есте плин де путере ши чел причепут ышь оцелеште влага.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
Кэч прин мэсурь кибзуите кыштиӂь бэтэлия, ши прин мареле нумэр ал сфетничилор ай бируинца.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Ынцелепчуня есте пря ыналтэ пентру чел небун: ел ну ва дескиде гура ла жудекатэ.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Чине се гындеште сэ факэ рэу се кямэ ун ом плин де рэутате.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Гындул челуй небун ну есте декыт пэкат ши батжокориторул есте о скырбэ пентру оамень.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Дакэ слэбешть ын зиуа неказулуй, микэ ыць есте путеря.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Избэвеште пе чей тырыць ла моарте ши скапэ пе чей че сунт апроапе сэ фие ынжунгияць.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Дакэ зичь: „Ах! н-ам штиут…”, крезь кэ ну веде Чел че кынтэреште инимиле ши Чел че вегязэ асупра суфлетулуй тэу? Ши ну ва рэсплэти Ел фиекэруя дупэ фаптеле луй?
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Фиуле, мэнынкэ мьере, кэч есте бунэ, ши фагуреле де мьере есте дулче пентру черул гурий тале!
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Тот аша ши ынцелепчуня есте бунэ пентру суфлетул тэу: дакэ о вей гэси, ай ун виитор ши ну ци се ва тэя нэдеждя.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Ну ынтинде курсе, нелеӂюитуле, ла локуинца челуй неприхэнит ши ну-й тулбура одихна!
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
Кэч чел неприхэнит де шапте орь каде ши се ридикэ, дар чей рэй се прэбушеск ын ненорочире.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Ну те букура де кэдеря врэжмашулуй тэу ши сэ ну ци се веселяскэ инима кынд се потикнеште ел,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
ка ну кумва Домнул сэ вадэ, сэ ну-Й плакэ ши сэ-Шь ынтоаркэ мыния де ла ел!
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Ну те мыния дин причина челор че фак рэу ши ну пизмуи пе чей рэй!
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
Кэч чел че фаче рэул н-аре ничун виитор ши лумина челор рэй се стинӂе.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Фиуле, теме-те де Домнул ши де ымпэратул ши сэ ну те аместечь ку чей неастымпэраць!
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
Кэч деодатэ ле ва вени пеиря. Ши чине поате шти сфыршитул амындурора?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
Ятэ че май спун ынцелепций: „Ну есте бине сэ ай ын ведере фаца оаменилор ын жудекэць.”
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
Пе чине зиче челуй рэу: „Ту ешть бун!” ыл блестемэ попоареле ши-л урэск нямуриле.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
Дар челор че жудекэ дрепт ле мерӂе бине ши о маре бинекувынтаре вине песте ей.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
Ун рэспунс бун есте ка ун сэрут пе бузе.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Везь-ць ынтый де требурь афарэ, ынгрижеште де лукрул кымпулуй, ши апой апукэ-те сэ-ць зидешть каса!
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Ну ворби ын кип ушуратик ымпотрива апроапелуй тэу; орь ай вря сэ ыншель ку бузеле тале?
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Ну зиче: „Кум мь-а фэкут ел, аша ам сэ-й фак ши еу, ый вой рэсплэти дупэ фаптеле луй!”
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Ам трекут пе лынгэ огорул унуй ленеш ши пе лынгэ вия унуй ом фэрэ минте.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
Ши ера нумай спинь, акоперит де мэрэчинь, ши зидул де пятрэ ера прэбушит.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
М-ам уйтат бине ши ку луаре аминте ши ам трас ынвэцэтурэ дин че ам вэзут.
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
„Сэ май дорм пуцин, сэ май аципеск пуцин, сэ май ынкручишез мыниле пуцин, ка сэ мэ одихнеск…”
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
Ши сэрэчия вине песте тине пе неаштептате, ка ун хоц, ши липса, ка ун ом ынармат.

< Miyambo 24 >