< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Ne irigykedjél a rosszaság embereire, és ne kívánkozzál velök lenni;
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
mert pusztítást gondol ki szívök és bajt beszélnek ajkaik.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Bölcsesség által épül fel a ház és értelem által szilárdul meg;
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
és tudás által telnek meg a kamarák, mindennemű drága és kedves vagyonnal.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Bölcs férfi hatalmas és a tudás embere bátor erejű.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
Mert útmutatásokkal viselhetsz háborút, és győzelem van a tanácsosok sokaságában.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Magas az oktalannak a bölcsesség: a kapuban nem nyitja meg a száját.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
A ki azon gondolkodik, hogy rosszat tegyen, azt fondorlatok emberének hívják.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Oktalanság gondolata a vétek, és utálata az embereknek a csúfoló.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Ha elernyedtél a szükség napján, szűknek bizonyult az erőd.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Mentsd meg a halálra vitteket, és a megölésre támolygókat hát ha elvonnád.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Ha azt mondod: lám nem tudtunk róla, nemde a szívek meghatározója, ő ügyel rá, és lelked megóvója – ő tudja, és viszonoz az embernek tette szerint.
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Egyél, fiam, mézet, mert jó, és színméz édes az ínyednek:
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
ilyen, tudd meg, a bölcsesség a te lelkednek; ha megtaláltad, van jövendő és reményed nem írtatik ki.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Ne leselkedjél, te gonosz, az igaznak hajlékára, ne pusztítsd el heverő helyét;
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
mert hétszer elesik az igaz, de fölkel, de a gonoszok megbotlanak a szerencsétlenségben.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Midőn elesik az ellenséged, ne örülj, s midőn megbotlik, ne vigadjon szíved;
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
nehogy lássa az Örökkévaló és rossznak tetszenék szemeiben és elfordítaná tőle haragját.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Ne gerjedj föl a gonosztevők ellen, ne irigykedjél a gonoszokra;
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
mert nem lesz jövendője a rossznak, a gonoszok mécsese kialszik.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Féljed az Örökkévalót, fiam, és a királyt, az elszakadókkal ne állj össze;
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
mert hírtelen támad szerencsétlenségük, és mindkettejük balvégzetét ki ismeri?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
Ezek is bölcsektől valók. Személyt válogatni az ítéletben nem jó.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
A ki azt mondja a gonosznak: igaz vagy, azt átkozzák a népek, szidják a nemzetek;
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
de a megfeddőknek kellemes lesz a dolguk, és reájuk száll a jónak áldása.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
Az ajkakat csókolja, a ki helyes szavakkal válaszol.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Készítsd el odakünn munkádat, és intézd el azt magadnak a mezőn; azután építsd fel házadat.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Ne légy ok nélkül tanú felebarátod ellen; vajon ámítanád-e ajkaiddal?
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Ne mondd: amint velem tett, úgy teszek ő vele, viszonzok az embernek tette szerint.
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Rest ember mezeje mellett mentem el, és esztelen ember szőlleje mellett;
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
s íme egészen benőtte a tövis, ellepte színét a csalán, és kőfala le volt rombolva.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Néztem én, ráfordítottam szívemet, láttam, tanulságot vettem.
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
Egy kis alvás, egy kis szendergés, egy kis kézösszekulcsolás, hogy feküdj;
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
majd el jön vándorként a te szegénységed és szűkölködésed, mint a pajzsos férfi.

< Miyambo 24 >