< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Ne jalouse pas les hommes d’iniquité; ne souhaite pas de frayer avec eux;
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
car leur cœur machine des ruines, et leurs lèvres débitent l’injustice.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
C’Est par la sagesse que s’édifie la maison c’est par la raison qu’elle se consolide.
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
Grâce à l’intelligence, le logis se remplit de toute sorte de biens rares et précieux.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Le sage est armé d’énergie, et l’homme d’expérience voit doubler sa force.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
C’Est en suivant un plan habile que tu dois entreprendre la guerre; la victoire est assurée par la multitude des conseillers.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Les données de la sagesse sont inaccessibles au sot; à la Porte, il n’ouvre pas la bouche.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Qui médite de faire le mal, on l’appelle l’homme aux noirs projets.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Le péché est une conception de la folie, et les gens ont horreur du persifleur.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Il faiblit au jour de la détresse: c’est que ton courage a l’haleine courte.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Sauve ceux qu’on traîne à la mort, ne manque pas de défendre ceux qui vont au supplice.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Tu diras peut-être: "Cet homme là, nous ne le connaissons pas!" Mais celui qui pénètre au. fond des cœurs comprend; celui qui veille sur ta vie sait, et il rétribue chacun selon ses œuvres.
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Mange du miel, mon fils, car c’est bon; les rayons en seront doux à ton palais.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Telle est, sache-le bien, la sagesse pour ton âme; si tu t’en rends maître, il y a de l’avenir pour toi, ton espoir ne sera pas anéanti.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Méchant, pas de machination secrète contre la demeure du juste! Pas d’entreprises contre le lieu de sa résidence!
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
Car le juste tombe sept fois, et se relève; mais les méchants sont culbutés par le malheur.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Lorsque ton ennemi tombe, ne te réjouis point; s’il succombe, que ton cœur ne jubile pas!
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
L’Eternel verrait cela de mauvais œil, et il détournerait de lui sa colère.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Ne porte pas envie aux malfaiteurs, ne jalouse pas les méchants;
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
car le méchant n’a pas d’avenir: la lumière des impies est fumeuse.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Crains l’Eternel, mon fils, ainsi que le roi: ne te mêle pas aux novateurs;
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
car soudain, le désastre fond sur eux: qui peut mesurer les coups que leur réservent l’un et l’autre?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
Les sentences suivantes émanent également des sages: Faire acception de personnes en justice n’est pas une bonne chose.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
Celui qui prononce sur le coupable en disant: "Tu es acquitté!" les peuples le maudissent, les gens l’exècrent.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
Mais on est bienveillant pour ceux qui le répriment, et il leur vient des souhaits de bonheur.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
C’Est comme un baiser des lèvres que de répliquer par dés paroles équitables.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Prépare-toi une occupation au dehors, déploie ton activité dans ton champ, puis, tu édifieras ta maison.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Ne témoigne pas sans motif contre ton prochain: prétendrais-tu exercer une séduction par tes lèvres?
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Ne dis pas: "Comme il m’a traité, je le traiterai; je rends à chacun selon ses œuvres."
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
J’Ai passé près du champ d’un paresseux, près du vignoble d’un homme privé de sens.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
Et voilà qu’il était tout envahi par l’ivraie; les ronces en recouvraient la surface, l’enclos de pierres était en ruines.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Je contemplai ce spectacle, j’y donnai mon attention, et de cette vue je tirai une leçon:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
"Ah! dormir encore un peu, rester un peu assoupi, entrelacer un peu les mains pour reposer!"
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
"Cependant, la pauvreté s’introduit chez toi comme un rôdeur, et la misère comme un guerrier armé!"

< Miyambo 24 >