< Miyambo 24 >
1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Be not thou enuious against euill men, neither desire to be with them.
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
For their heart imagineth destruction, and their lippes speake mischiefe.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Through wisdome is an house builded, and with vnderstanding it is established.
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
And by knowledge shall the chambers bee filled with all precious, and pleasant riches.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
A wise man is strong: for a man of vnderstanding encreaseth his strength.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
For with counsel thou shalt enterprise thy warre, and in the multitude of them that can giue counsell, is health.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Wisdome is hie to a foole: therefore he can not open his mouth in the gate.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Hee that imagineth to doe euill, men shall call him an autour of wickednes.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
The wicked thought of a foole is sinne, and the scorner is an abomination vnto men.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
If thou bee faint in the day of aduersitie, thy strength is small.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Deliuer them that are drawen to death: wilt thou not preserue them that are led to be slaine?
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
If thou say, Beholde, we knew not of it: he that pondereth the heartes, doeth not hee vnderstand it? and hee that keepeth thy soule, knoweth he it not? will not he also recompense euery man according to his workes?
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
My sonne, eate hony, for it is good, and the hony combe, for it is sweete vnto thy mouth.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
So shall the knowledge of wisdome be vnto thy soule, if thou finde it, and there shall be an ende, and thine hope shall not be cut off.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Laye no waite, O wicked man, against the house of the righteous, and spoyle not his resting place.
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
For a iust man falleth seuen times, and riseth againe: but the wicked fall into mischiefe.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Bee thou not glad when thine enemie falleth, and let not thine heart reioyce when hee stumbleth,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
Least the Lord see it, and it displease him, and he turne his wrath from him.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Fret not thy selfe because of the malicious, neither be enuious at the wicked.
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
For there shall bee none ende of plagues to the euill man: the light of the wicked shall bee put out.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
My sonne feare the Lord, and the King, and meddle not with them that are sedicious.
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
For their destruction shall rise suddenly, and who knoweth the ruine of them both?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
ALSO THESE THINGS PERTEINE TO THE WISE, It is not good to haue respect of any person in iudgement.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
He that saith to the wicked, Thou art righteous, him shall the people curse, and the multitude shall abhorre him.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
But to them that rebuke him, shall be pleasure, and vpon them shall come the blessing of goodnesse.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
They shall kisse the lippes of him that answereth vpright wordes.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Prepare thy worke without, and make readie thy thinges in the fielde, and after, builde thine house.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Be not a witnes against thy neighbour without cause: for wilt thou deceiue with thy lippes?
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Say not, I wil doe to him, as he hath done to mee, I will recompence euery man according to his worke.
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
I passed by the fielde of the slouthfull, and by the vineyarde of the man destitute of vnderstanding.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
And lo, it was al growen ouer with thornes, and nettles had couered the face thereof, and the stone wall thereof was broken downe.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Then I behelde, and I considered it well: I looked vpon it, and receiued instruction.
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
Yet a litle sleepe, a litle slumber, a litle folding of the handes to sleepe.
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
So thy pouertie commeth as one that traueileth by the way, and thy necessitie like an armed man.