< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
[My] son, envy not bad men, nor desire to be with them.
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
For their heart meditates falsehoods, and their lips speak mischiefs.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
A house is built by wisdom, and is set up by understanding.
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
By discretion the chambers are filled with all precious and excellent wealth.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
A wise man is better than a strong man; and a man who has prudence than a large estate.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
War is carried on with generalship, and aid is supplied to the heart of a counsellor.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Wisdom and good understanding are in the gates of the wise: the wise turn not aside from the mouth of the Lord,
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
but deliberate in council. Death befalls uninstructed [men].
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
The fools also dies in sins; and uncleanness [attaches] to a pestilent man.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
He shall be defiled in the evil day, and in the day of affliction, until he be utterly consumed.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Deliver them that are led away to death, and redeem them that are appointed to be slain; spare not [thy help].
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
But if thou shouldest say, I know not this man; know that the Lord knows the hearts of all; and he that formed breath for all, he knows all things, who renders to every man according to his works.
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
[My] son, eat honey, for the honeycomb is good, that thy throat may be sweetened.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Thus shalt thou perceive wisdom in thy soul: for if thou find it, thine end shall be good, and hope shall not fail thee.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Bring not an ungodly man into the dwelling of the righteous: neither be deceived by the feeding of the belly.
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
For a righteous man will fall seven times, and rise [again]: but the ungodly shall be without strength in troubles.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
If thine enemy should fall, rejoice not over him, neither be elated at his overthrow.
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
For the Lord will see [it], and it will not please him, and he will turn away his wrath from him.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Rejoice not in evil-doers, neither be envious of sinners.
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
For the evil man shall have no posterity: and the light of the wicked shall be put out.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
[My] son, fear God and the king; and do not disobey either of them.
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
For they will suddenly punish the ungodly, and who can know the vengeance [inflicted] by both?
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
And this thing I say to you that are wise [for you] to learn: It is not good to have respect of persons in judgment.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
He that says of the ungodly, He is righteous, shall be cursed by peoples, and hateful among the nations.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
But they that reprove [him] shall appear more excellent, and blessing shall come upon them;
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
and [men] will kiss lips that answer well.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Prepare thy works for [thy] going forth, and prepare thyself for the field; and come after me, and thou shalt rebuild thine house.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Be not a false witness against thy [fellow] citizen, neither exaggerate with thy lips.
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Say not, As he has treated me, so will I treat him, and I will avenge myself on him for that wherein he has injured me.
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
A foolish man is like a farm, and a senseless man is like a vineyard.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
If thou let him alone, he will altogether remain barren and covered with weeds; and he becomes destitute, and his stone walls are broken down.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Afterwards I reflected, I looked that I might receive instruction.
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
[The sluggard says, ]I slumber a little, and I sleep a little, and for a little while I fold my arms across [my] breast.
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
But if thou do this, thy poverty will come speedily; and thy want like a swift courier.

< Miyambo 24 >