< Miyambo 24 >

1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Misund ej onde Folk, hav ikke lyst til at være med dem;
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
thi deres Hjerte pønser paa Vold, deres Læbers Ord volder Men.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Ved Visdom bygges et Hus, ved Indsigt holdes det oppe,
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
ved Kundskab fyldes Kamrene med alskens kosteligt, herligt Gods.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Vismand er større end Kæmpe, kyndig Mand mer end Kraftkarl.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
Thi Krig skal du føre efter modent Overlæg, vel staar det til, hvor mange giver Raad.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Visdom er Daaren for høj, han aabner ej Munden i Porten.
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Den, der har ondt i Sinde, kaldes en rænkefuld Mand.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Hvad en Daare har for, er Synd, en Spotter er Folk en Gru.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Taber du Modet paa Trængslens Dag, da er din Kraft kun ringe.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Frels dem, der slæbes til Døden, red dem, der vakler hen for at dræbes.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Siger du: »Se, jeg vidste det ikke« — mon ej han, der vejer Hjerter, kan skønne? Han, der tager Vare paa din Sjæl, han ved det, han gengælder Mennesker, hvad de har gjort.
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Spis Honning, min Søn, det er godt, og Kubens Saft er sød for din Gane;
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
vid, at saa er og Visdom for Sjælen! Naar du finder den, har du en Fremtid, dit Haab bliver ikke til intet.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Lur ej paa den retfærdiges Bolig, du gudløse, ødelæg ikke hans Hjem;
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
thi syv Gange falder en retfærdig og staar op, men gudløse styrter i Fordærv.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Falder din Fjende, saa glæd dig ikke, snubler han, juble dit Hjerte ikke,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
at ikke HERREN skal se det med Mishag og vende sin Vrede fra ham.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Græm dig ej over Ugerningsmænd, misund ikke de gudløse;
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
thi den onde har ingen Fremtid, gudløses Lampe gaar ud.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Frygt HERREN og Kongen, min Søn, indlad dig ikke med Folk, som gør Oprør;
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
thi brat kommer Ulykke fra dem, uventet Fordærv fra begge.
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
Ogsaa følgende Ordsprog er af vise Mænd. Partiskhed i Retten er ilde.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
Mod den, som kender en skyldig fri, er Folkeslags Banden, Folkefærds Vrede;
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
men dem, der dømmer med Ret, gaar det vel, dem kommer Lykkens Velsignelse over.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
Et Kys paa Læberne giver den, som kommer med ærligt Svar.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Fuldfør din Gerning udendørs, gør dig færdig ude paa Marken og byg dig siden et Hus!
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Vidn ikke falsk mod din Næste, vær ikke letsindig med dine Læber;
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
sig ikke: »Jeg gør mod ham, som han gjorde mod mig, jeg gengælder hver hans Gerning.«
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Jeg kom forbi en lad Mands Mark og et uforstandigt Menneskes Vingaard;
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
se, den var overgroet af Tidsler, ganske skjult af Nælder; Stendiget om den laa nedbrudt.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Jeg skued og skrev mig det bag Øre, jeg saa og tog Lære deraf:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
Lidt Søvn endnu, lidt Blund, lidt Hvile med samlagte Hænder:
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
Som en Stimand kommer da Fattigdom over dig, Trang som en skjoldvæbnet Mand.

< Miyambo 24 >