< Miyambo 24 >
1 Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
Ne zavidi opakim ljudima niti želi da budeš s njima.
2 pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
Jer im srce smišlja nasilje i usne govore o nedjelu.
3 Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Mudrošću se zida kuća i razborom utvrđuje,
4 Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
i po znanju se pune klijeti svakim blagom dragocjenim i ljupkim.
5 Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Bolji je mudar od jakoga i čovjek razuman od silne ljudine.
6 Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
Jer s promišljanjem se ide u boj i pobjeda je u mnoštvu savjetnika.
7 Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
Previsoka je bezumnomu mudrost: zato na sudu ne otvara usta svojih!
8 Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
Tko smišlja zlo zove se učitelj podmukli.
9 Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
Ludost samo grijeh snuje, i podrugljivac je mrzak ljudima.
10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
Kloneš li u dan bijede, bijedna je tvoja snaga.
11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
Izbavi one koje vode u smrt; i spasavaj one koji posrćući idu na stratište.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
Ako kažeš: “Nismo za to znali”, ne razumije li onaj koji ispituje srca? I ne znade li onaj koji ti čuva dušu? I ne plaća li on svakomu po njegovim djelima?
13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
Jedi med, sine moj, jer je dobar, i saće je slatko nepcu tvome.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
Takva je, znaj, i mudrost tvojoj duši: ako je nađeš, našao si budućnost i nada tvoja neće propasti.
15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
Ne postavljaj, opaki, zasjede stanu pravednikovu, ne čini nasilja boravištu njegovu;
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
jer padne li pravednik i sedam puta, on ustaje, a opaki propadaju u nesreći.
17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
Ne veseli se kad padne neprijatelj tvoj i ne kliči srcem kada on posrće,
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
da ne bi vidio Jahve i za zlo uzeo i obratio srdžbu svoju od njega.
19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
Nemoj se srditi zbog zločinaca, nemoj zavidjeti opakima,
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
jer zao čovjek nema budućnosti, svjetiljka opakih gasi se.
21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
Boj se Jahve, sine moj, i kralja: i ne buni se ni protiv jednoga ni protiv drugoga.
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
Jer iznenada provaljuje nesreća njihova i tko zna kad će doći propast njihova.
23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
I ovo je od mudraca: Ne valja biti pristran na sudu.
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
Tko opakomu veli: “Pravedan si”, proklinju ga narodi i kunu puci;
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
a oni koji ga ukore nalaze zadovoljstvo, i na njih dolazi blagoslov sreće.
26 Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
U usta ljubi tko odgovara pošteno.
27 Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
Svrši svoj posao vani i uredi svoje polje, potom i kuću svoju zidaj.
28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
Ne svjedoči lažno na bližnjega svoga: zar ćeš varati usnama svojim?
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
Ne reci: “Kako je on meni učinio, tako ću i ja njemu; platit ću tom čovjeku po djelu njegovu!”
30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
Prolazio sam mimo polje nekog lijenčine i mimo vinograd nekog luđaka,
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
i gle, sve bijaše zaraslo u koprive, i sve pokrio čkalj, i kamena ograda porušena.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
Vidjeh to i pohranih u srcu, promotrih i uzeh pouku:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
“Još malo odspavaj, još malo odrijemaj, još malo podvij ruke za počinak,
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.
i doći će tvoje siromaštvo kao skitač i oskudica kao oružanik!”