< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Коли сядеш хліб їсти з воло́дарем, то пильно вважай, що́ перед тобою, —
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
і поклади собі в горло ножа, якщо ти ненаже́ра:
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
не жадай його ласощів, бо вони — хліб обма́нливий!
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Не мордуйся, щоб мати багатство, — відступи́ся від ду́мки своєї про це, —
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
свої очі ти зве́рнеш на нього, — й нема вже його: бо конче змайструє воно собі кри́ла, і полетить, мов орел той, до неба.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
не їж хліба в злоокого, і не пожада́й лакоми́нок його,
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
бо як у душі своїй він обрахо́вує, такий є. Він скаже тобі: „їж та пий!“, але серце його не з тобою, —
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
той кава́лок, якого ти з'їв, із себе ви́кинеш, і свої гарні слова́ надаремно потра́тиш!
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Не кажи до ушей нерозумному, бо пого́рдить він мудрістю слів твоїх.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Не пересува́й віково́ї границі, і не входь на сирі́тські поля́,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
бо їхній Визволи́тель міцни́й, — Він за справу їхню буде суди́тись з тобою!
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Своє серце зверни до навча́ння, а уші свої — до розумних рече́й.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Не стримуй напу́чування юнака́, — коли різкою ви́б'єш його, не помре:
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
ти різкою виб'єш його, — і душу його від шео́лу врятуєш. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Мій сину, якщо твоє серце змудріло, то буде радіти також моє серце,
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
і нутро́ моє буде ті́шитись, коли уста твої говори́тимуть слу́шне.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Нехай серце твоє не зави́дує грішним, і повся́кчас пильнуй тільки стра́ху Господнього,
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
бо існує майбутнє, і наді́я твоя не загине.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Послухай, мій сину, та й помудрі́й, і нехай твоє серце ступає дорогою рівною.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Не будь поміж тими, що жлу́ктять вино, поміж тими, що м'ясо собі пожира́ють,
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
бо п'яни́ця й жеру́н збідні́ють, а сонли́вий одя́гне лахмі́ття.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Слухай ба́тька свого, — він тебе породив, і не горду́й, як поста́ріла мати твоя.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Купи собі й не продавай правду, мудрість, і карта́ння та розум.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Буде ве́льми радіти ба́тько праведного, і родитель премудрого вті́шиться ним.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Хай радіє твій ба́тько та мати твоя, хай поті́шиться та, що тебе породила.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Дай мені, сину мій, своє серце, і очі твої хай кохають доро́ги мої.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Бо блудни́ця — то яма глибока, а крини́ця тісна́ — чужа жінка.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
І вона, мов грабі́жник, чату́є, і примно́жує зра́дників поміж людьми́.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
В кого „ой“, в кого „ай“, в кого сва́рки, в кого кло́піт, в кого рани даре́мні, в кого о́чі червоні? —
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
У тих, хто запі́знюється над вином, у тих, хто прихо́дить попро́бувати вина змі́шаного.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Не дивись на вино, як воно рум'яні́є, як вибли́скує в келіху й рі́вненько ллється, —
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
кінець його буде кусати, як гад, і вжа́лить, немов та гадюка, —
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
пантрува́тимуть очі твої на чужі жінки, і серце твоє говори́тиме ду́рощі...
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
І ти будеш, як той, хто лежить у сере́дині моря, й як той, хто лежить на щогло́вім верху́.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
І скажеш: „Побили мене, та мені не боліло, мене шту́рхали, я ж не почув, — коли я прокинусь, шукатиму далі того ж“.

< Miyambo 23 >