< Miyambo 23 >
1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Uketipo kula chakula na mtawala, angalia vyema kile kilicho mbele yako,
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
na utie kisu kooni mwako kama ukiwa mlafi.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Usitamani vyakula vyake vitamu kwa kuwa chakula hicho ni cha hila.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Usijitaabishe ili kuupata utajiri, uwe na hekima kuonyesha kujizuia.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Kufumba na kufumbua utajiri hutoweka, huwa kama umepata mabawa ghafula, ukaruka na kutoweka angani kama tai.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Usile chakula cha mtu mchoyo, usitamani vyakula vyake vitamu,
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
kwa maana yeye ni aina ya mtu ambaye kila mara anafikiri juu ya gharama. Anakuambia, “Kula na kunywa,” lakini moyo wake hauko pamoja nawe.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Utatapika kile kidogo ulichokula, nawe utakuwa umepoteza bure maneno yako ya kumsifu.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Usizungumze na mpumbavu, kwa maana atadhihaki hekima ya maneno yako.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Usisogeze jiwe la mpaka wa zamani wala kunyemelea kwenye mashamba ya yatima,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
kwa kuwa Mtetezi wao ni mwenye nguvu, atalichukua shauri lao dhidi yako.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Elekeza moyo wako kwenye mafundisho na masikio yako kwenye maneno ya maarifa.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Usimnyime mtoto adhabu, ukimwadhibu kwa fimbo, hatakufa.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
Mwadhibu kwa fimbo na kuiokoa nafsi yake kutoka mautini. (Sheol )
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Mwanangu, kama moyo wako una hekima, basi moyo wangu utafurahi,
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
utu wangu wa ndani utafurahi, wakati midomo yako itakapozungumza lililo sawa.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Usiuruhusu moyo wako kuwaonea wivu wenye dhambi, bali kila mara uwe na bidii katika kumcha Bwana.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
Hakika kuna tumaini la baadaye kwa ajili yako, nalo tarajio lako halitakatiliwa mbali.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Sikiliza, mwanangu na uwe na hekima, weka moyo wako kwenye njia iliyo sawa.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Usiwe miongoni mwa wanywao mvinyo, au wale walao nyama kwa pupa,
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
kwa maana walevi na walafi huwa maskini, nako kusinzia huwavika matambara.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Msikilize baba yako, aliyekuzaa, wala usimdharau mama yako atakapokuwa mzee.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Nunua kweli wala usiiuze, pata hekima, adabu na ufahamu.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Baba wa mwenye haki ana furaha kubwa, naye aliye na mwana mwenye hekima humfurahia.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Baba yako na mama yako na wafurahi, mama aliyekuzaa na ashangilie!
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Mwanangu, nipe moyo wako, macho yako na yafuate njia zangu,
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
kwa maana kahaba ni shimo refu na mwanamke mpotovu ni kisima chembamba.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Kama mnyangʼanyi, hungojea akivizia, naye huzidisha wasio waaminifu miongoni mwa wanaume.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Ni nani mwenye ole? Ni nani mwenye huzuni? Ni nani mwenye ugomvi? Ni nani mwenye malalamiko? Ni nani aliye na majeraha yasiyo na sababu? Ni nani mwenye macho mekundu?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Ni hao wakaao sana kwenye mvinyo, hao waendao kuonja mabakuli ya mvinyo uliochanganywa.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Usiukodolee macho mvinyo wakati ukiwa mwekundu, wakati unapometameta kwenye bilauri, wakati ushukapo taratibu!
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
Mwishowe huuma kama nyoka na kutia sumu yake kama nyoka mwenye sumu.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Macho yako yataona mambo mageni na moyo wako kuwazia mambo yaliyopotoka.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Utakuwa kama alalaye katikati ya bahari, alalaye juu ya kamba ya merikebu.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
Utasema, “Wamenipiga lakini sikuumia! Wamenichapa, lakini sisikii! Nitaamka lini ili nikanywe tena?”