< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Дакэ стай ла масэ ла унул дин чей марь, я сяма че ай динаинте:
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
пуне-ць ун куцит ын гыт, дакэ ешть пря лаком.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Ну пофти мынкэруриле луй алесе, кэч сунт о хранэ ыншелэтоаре!
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Ну те кинуи ка сэ те ымбогэцешть, ну-ць пуне причеперя ын ачаста!
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Абя ць-ай арункат окий спре еа, ши ну май есте; кэч богэция ышь фаче арипь ши, ка вултурул, ышь я зборул спре черурь.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Ну мынка пыня челуй пизмаш ши ну пофти мынкэруриле луй алесе,
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
кэч ел есте ка унул каре ышь фаче сокотелиле ын суфлет! „Мэнынкэ ши бя”, ыць ва зиче ел, дар инима луй ну есте ку тине.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Буката пе каре ай мынкат-о о вей вэрса ши кувинтеле плэкуте пе каре ле вей спуне сунт пердуте.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Ну ворби ла урекя челуй небун, кэч ел несокотеште кувинтеле тале ынцелепте!
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Ну мута хотарул вэдувей ши ну интра ын огорул орфанилор,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
кэч Рэзбунэторул лор есте путерник: Ел ле ва апэра причина ымпотрива та.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Дескиде-ць инима ла ынвэцэтурэ ши урекиле ла кувинтеле штиинцей!
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Ну круца копилул де мустраре, кэч, дакэ-л вей лови ку нуяуа, ну ва мури!
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Ловинду-л ку нуяуа, ый скоць суфлетул дин Локуинца морцилор. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Фиуле, дакэ-ць ва фи инима ынцеляптэ, инима мя се ва букура;
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
ши лэунтрул меу се ва весели кынд бузеле тале вор спуне че есте бине.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Сэ ну-ць пизмуяскэ инима пе чей пэкэтошь, чи сэ айбэ тотдяуна фрикэ де Домнул,
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
кэч есте о рэсплатэ ши ну ци се ва тэя нэдеждя.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Аскултэ, фиуле, ши фий ынцелепт; ындряптэ-ць инима пе каля чя дряптэ!
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Ну фи принтре чей че бяу вин, нич принтре чей че се ымбуйбэ ку карне!
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
Кэч бецивул ши чел че се дедэ ла ымбуйбаре сэрэческ, ши аципиря те фаче сэ порць здренце.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Аскултэ пе татэл тэу, каре те-а нэскут, ши ну несокоти пе мамэ-та кынд а ымбэтрынит.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Кумпэрэ адевэрул – ши ну-л винде –, ынцелепчуня, ынвэцэтура ши причеперя.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Татэл челуй неприхэнит се веселеште ши чел че дэ наштере унуй ынцелепт се букурэ.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Сэ се букуре татэл тэу ши мама та, сэ се веселяскэ чя каре те-а нэскут.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Фиуле, дэ-Мь инима та ши сэ гэсяскэ плэчере окий тэй ын кэиле Меле!
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Кэч курва есте о гроапэ адынкэ ши стрэина, о фынтынэ стрымтэ.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Еа пындеште ка ун хоц ши мэреште ынтре оамень нумэрул челор стрикаць.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Але куй сунт ваетеле? Але куй сунт офтэриле? Але куй сунт неынцелеӂериле? Але куй сунт плынӂериле? Але куй сунт рэнириле фэрэ причинэ? Ай куй сунт окий роший?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Але челор че ынтырзие ла вин ши се дук сэ голяскэ пахарул ку вин аместекат.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Ну те уйта ла вин кынд курӂе рошу ши фаче мэргэритаре ын пахар; ел алунекэ ушор,
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
дар пе урмэ ка ун шарпе мушкэ ши ынцяпэ ка ун басилиск.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Окий ци се вор уйта дупэ фемеиле алтора ши инима ыць ва ворби простий.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Вей фи ка ун ом кулкат ын мижлокул мэрий, ка ун ом кулкат пе вырфул унуй катарг.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
„М-а ловит …, дар ну мэ доаре!… М-а бэтут…, дар ну симт нимик! Кынд мэ вой трези? Май вряу вин!”

< Miyambo 23 >