< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Bw’otuulanga okulya n’omufuzi, weetegerezanga ebiri mu maaso go;
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
era weegendereze bw’obanga omanyi ng’olulunkanira ebyokulya.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Tolulunkanira mmere ye ennungi, kubanga erimbalimba.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Teweemalangako mirembe ng’oyaayaanira obugagga; weefuge obeere mukkakkamu.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Eby’obugagga obikubako eriiso limu nga by’agenze dda, kubanga ddala bimera ebiwaawaatiro ne bibuuka mu bbanga ng’empungu.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Tolyanga mmere ya muntu mukodo, wadde okwegomba ebirungi by’alya.
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
Kubanga ye muntu abalirira ensimbi z’asaasaanyizza, n’akugamba nti, “Weeriire, weenywere,” naye ng’omutima gwe tegukusanyukira.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Akatono k’onooba olidde onookasesema, ebigambo byo ebirungi eby’okwebaza bibe bya bwereere.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Totegana kubuulirira musirusiru, kubanga ajja kunyooma ebigambo byo eby’amagezi.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Tojjululanga nsalo ey’edda, so toyingiriranga nnimiro za bamulekwa,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
kubanga abalwanirira w’amaanyi, alikuggulako omusango.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Ossangayo omwoyo eri okuyigirizibwa, n’amatu go eri ebigambo by’okutegeera.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Tolekangayo kukangavvula mwana, bw’omubonereza n’akaggo tekimutta.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Mubonerezenga n’akaggo, kiwonye emmeeme ye okufa. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Mwana wange, bw’oba n’omutima ogw’amagezi, kinsanyusa.
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
Nnaajjaguzanga okuva ku ntobo y’omutima gwange, bw’onooyogeranga ebituufu.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Omutima gwo gulemenga okukwatirwa aboonoonyi obuggya, kyokka nyiikira okutya Mukama ebbanga lyonna.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
Mazima ddala onoobanga n’essuubi mu biseera eby’omu maaso, n’essuubi lyo eryo teririggwaawo.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Mwana wange wulirizanga, obeerenga n’amagezi, okumenga omutima gwo mu kkubo ettuufu.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Teweegattanga ku abo abeekamirira omwenge, n’abalulunkanira ennyama:
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
Kubanga omutamiivu n’omuluvu baavuwala, n’okubongoota olutata kubambaza enziina.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Wulirizanga kitaawo eyakuzaala, so togayanga nnyoko ng’akaddiye.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Gula amazima so togatunda, ffuna amagezi, n’okuyigirizibwa n’okutegeera.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Kitaawe w’omutuukirivu alina essanyu lingi, n’oyo azaala omwana ow’amagezi amwenyumiririzaamu.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Leka kitaawo ne nnyoko basanyuke, omukazi eyakuzaala ajaguzenga.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Mwana wange mpa omutima gwo, n’amaaso go geekalirize amakubo gange,
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
kubanga omukazi omwenzi lukonko luwanvu, n’omukazi omubambaavu luzzi lufunda.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Ateega ng’omutemu, n’ayongera ku muwendo gw’abasajja abatali beesigwa eri bakazi baabwe.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Ani alina obuyinike? Ani alina ennaku? Ani alina ennyombo? Ani alina okwemulugunya? Ani alina ebiwundu eby’obwereere? Ani amyuse amaaso?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Abo abatava ku mwenge, nga bagenda baloza ku mwenge omutabule.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Totunuulira wayini ng’amyuse, bw’atemaganira mu ggiraasi ng’akka empolampola;
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
ku nkomerero aluma ng’omusota, wa busagwa ng’essalambwa.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Amaaso go galiraba ebyewuunyo, n’omutwe gwo ne gulowooza ebitategeerekeka.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Oliba ng’omuntu eyeebase wakati mu nnyanja, obanga oyo alengejjera waggulu ku mulongooti.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
Olyogera nti, “Bankubye, naye sirumiddwa. Bankubye naye sirina kye mpuliddemu. Nnaazuukuka ddi, neeyongere okunywa?”

< Miyambo 23 >