< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Si tu t'assieds à table avec un prince, considère bien qui tu as devant toi,
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
et mets un couteau à ton gosier, si tu as un appétit trop grand!
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Ne convoite point ses friandises, car c'est un mets trompeur.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Ne t'efforce pas de l'enrichir, renonce à être si prudent!
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Tes regards voltigeront-ils vers ce qui va n'être plus? car il prendra des ailes, comme l'aigle et les oiseaux du ciel.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Ne mange pas le pain de l'avare, et ne convoite pas ses friandises!
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
Car il est ce qu'il est en son cœur, calculateur. Mange et bois! te dira-t-il; mais son cœur n'est pas avec toi;
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
tu rejetteras le morceau que tu auras mangé, et tu auras tenu en pure perte d'agréables propos.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Aux oreilles de l'insensé ne parle pas, car il méprise la sagesse de tes discours.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Ne déplace point la borne antique, et n'envahis point le champ de l'orphelin!
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
Car son vengeur est puissant, et Il prendra son parti contre toi.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Présente ton cœur à la correction, et tes oreilles aux discours de la sagesse.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
N'épargne pas la correction au jeune enfant! Si tu le frappes de la verge, il ne mourra point.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
En le frappant de la verge tu sauves son âme des Enfers. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Mon fils, si ton cœur est sage, mon cœur, oui, mon cœur sera dans la joie;
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
l'allégresse pénétrera mes entrailles, si tes lèvres parlent avec rectitude.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Que ton cœur n'envie pas les pécheurs, mais qu'il garde toujours la crainte de l'Éternel.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
Non! car il est un avenir, et ton espoir ne sera pas mis à néant.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Ecoute, mon fils, et sois sage, et dirige ton cœur dans le droit chemin.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Ne sois point parmi les buveurs de vin, et ceux qui sont prodigues de leur corps;
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
car le buveur et le prodigue s'appauvrissent, et l'assoupissement revêt de haillons.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Obéis à ton père, il t'a engendré, et ne méprise point ta mère devenue vieille.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Achète la vérité, et ne la vends pas, la sagesse, la discipline et le sens.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Le père du juste est dans l'allégresse, et celui qui a engendré un sage, en recueille de la joie.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Puisses-tu réjouir ton père et ta mère, et être l'allégresse de celle qui te donna naissance!
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Donne-moi ton cœur, mon fils, et que mes voies plaisent à tes yeux!
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Car la courtisane est une fosse profonde, et l'étrangère, un puits étroit;
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
elle épie, comme un ravisseur, et augmente parmi les hommes le nombre des infidèles.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Pour qui sont les ah? pour qui les hélas? pour qui les rixes? pour qui le chagrin? pour qui les coups non provoqués? pour qui les yeux troubles.
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Pour ceux qui boivent longuement, qui viennent déguster le vin parfumé.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Ne regarde pas le vin, quand il est vermeil, quand dans la coupe il élève ses bulles, et que sa liqueur est flatteuse!
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
Il finit par blesser comme le serpent, et par piquer, comme la vipère.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Tes yeux alors se porteront sur les étrangères, et ton cœur tiendra un langage pervers;
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
et tu seras comme celui qui dort en pleine mer, comme celui qui dort à la cime du mât.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
« Ils me battent; cela ne fait pas mal: ils me frappent; je ne sens rien. Quand me réveillerai-je? J'y veux retourner. »

< Miyambo 23 >