< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Whanne thou sittist, to ete with the prince, perseyue thou diligentli what thingis ben set bifore thi face,
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
and sette thou a withholding in thi throte. If netheles thou hast power on thi soule,
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
desire thou not of his metis, in whom is the breed of `a leesing.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Nyle thou trauele to be maad riche, but sette thou mesure to thi prudence.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Reise not thin iyen to richessis, whiche thou maist not haue; for tho schulen make to hem silf pennes, as of an egle, and tho schulen flee in to heuene.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Ete thou not with an enuyouse man, and desire thou not hise metis;
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
for at the licnesse of a fals dyuynour and of a coniectere, he gessith that, that he knowith not. He schal seie to thee, Ete thou and drinke; and his soule is not with thee.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Thou schalt brake out the metis, whiche thou hast ete; and thou schalt leese thi faire wordis.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Speke thou not in the eeris of vnwise men; for thei schulen dispise the teching of thi speche.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Touche thou not the termes of litle children; and entre thou not in to the feeld of fadirles and modirles children.
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
For the neiybore of hem is strong, and he schal deme her cause ayens thee.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Thin herte entre to techyng, and thin eeris `be redi to the wordis of kunnyng.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Nile thou withdrawe chastisyng fro a child; for thouy thou smyte hym with a yerde, he schal not die.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Thou schalt smyte hym with a yerde, and thou schalt delyuere his soule fro helle. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Mi sone, if thi soule is wijs, myn herte schal haue ioye with thee;
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
and my reynes schulen make ful out ioye, whanne thi lippis speken riytful thing.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Thin herte sue not synneris; but be thou in the drede of the Lord al dai.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
For thou schalt haue hope at the laste, and thin abidyng schal not be don awei.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Mi sone, here thou, and be thou wijs, and dresse thi soule in the weie.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Nyle thou be in the feestis of drinkeris, nether in the ofte etyngis of hem, that bryngen togidere fleischis to ete.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
For men yyuynge tent to drinkis, and yyuyng mussels togidere, schulen be waastid, and napping schal be clothid with clothis.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Here thi fadir, that gendride thee; and dispise not thi modir, whanne sche is eld.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Bie thou treuthe, and nyle thou sille wisdom, and doctryn, and vndurstonding.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
The fadir of a iust man ioieth ful out with ioie; he that gendride a wijs man, schal be glad in hym.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Thi fadir and thi modir haue ioye, and he that gendride thee, make ful out ioye.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
My sone, yyue thin herte to me, and thin iyen kepe my weyes.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
For an hoore is a deep diche, and an alien womman is a streit pit.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Sche settith aspie in the weie, as a theef; and sche schal sle hem, whiche sche schal se vnwar.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
To whom is wo? to whos fadir is wo? to whom ben chidingis? to whom ben dichis? to whom ben woundis with out cause? to whom is puttyng out of iyen?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Whether not to hem, that dwellen in wyn, and studien to drynke al of cuppis?
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Biholde thou not wyn, whanne it sparclith, whanne the colour therof schyneth in a ver.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
It entrith swetli, but at the laste it schal bite as an eddre doith, and as a cocatrice it schal schede abrood venyms.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Thin iyen schulen se straunge wymmen, and thi herte schal speke weiwerd thingis.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
And thou schalt be as a man slepinge in the myddis of the see, and as a gouernour aslepid, whanne the steere is lost.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
And thou schalt seie, Thei beeten me, but Y hadde not sorewe; thei drowen me, and Y feelide not; whanne schal Y wake out, and Y schal fynde wynes eft?

< Miyambo 23 >