< Miyambo 23 >
1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
When thou sittest to eat with a ruler, consider diligently him that is before thee;
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
And put a knife to thy throat, if thou be a man given to appetite.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Be not desirous of his dainties; seeing they are deceitful meat.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Weary not thyself to be rich; cease from thine own wisdom.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Wilt thou set thine eyes upon that which is not? for [riches] certainly make themselves wings, like an eagle that flieth toward heaven.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Eat thou not the bread of him that hath an evil eye, neither desire thou his dainties:
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
For as he reckoneth within himself, so is he: Eat and drink, saith he to thee; but his heart is not with thee.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
The morsel which thou hast eaten shalt thou vomit up, and lose thy sweet words.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Speak not in the hearing of a fool; for he will despise the wisdom of thy words.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Remove not the ancient landmark; and enter not into the fields of the fatherless:
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
For their redeemer is strong; he shall plead their cause against thee.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Apply thine heart unto instruction, and thine ears to the words of knowledge.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Withhold not correction from the child: [for] if thou beat him with the rod, he shall not die.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
Thou shalt beat him with the rod, and shalt deliver his soul from Sheol. (Sheol )
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
My son, if thine heart be wise, my heart shall be glad, even mine:
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
Yea, my reins shall rejoice, when thy lips speak right things.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Let not thine heart envy sinners: but [be thou] in the fear of the LORD all the day long:
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
For surely there is a reward; and thy hope shall not be cut off.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Hear thou, my son, and be wise, and guide thine heart in the way.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Be not among winebibbers; among gluttonous eaters of flesh:
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
For the drunkard and the glutton shall come to poverty: and drowsiness shall clothe [a man] with rags.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Hearken unto thy father that begat thee, and despise not thy mother when she is old.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Buy the truth, and sell it not; [yea], wisdom, and instruction, and understanding.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
The father of the righteous shall greatly rejoice: and he that begetteth a wise child shall have joy of him.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Let thy father and thy mother be glad, and let her that bare thee rejoice.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
My son, give me thine heart, and let thine eyes delight in my ways.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
For a whore is a deep ditch; and a strange woman is a narrow pit.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Yea, she lieth in wait as a robber, and increaseth the treacherous among men.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Who hath woe? who hath sorrow? who hath contentions? who hath complaining? who hath wounds without cause? who hath redness of eyes?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
They that tarry long at the wine; they that go to seek out mixed wine.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Look not thou upon the wine when it is red, when it giveth its colour in the cup, when it goeth down smoothly.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
At the last it biteth like a serpent, and stingeth like an adder.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Thine eyes shall behold strange things, and thine heart shall utter froward things.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Yea, thou shalt be as he that lieth down in the midst of the sea, or as he that lieth upon the top of a mast.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
They have stricken me, [shalt thou say], and I was not hurt; they have beaten me, and I felt it not: when shall I awake? I will seek it yet again.