< Miyambo 23 >
1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
When you sit to eat with a ruler, consider diligently what is before you;
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
put a knife to your throat, if you are a man given to appetite.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Do not be desirous of his dainties, seeing they are deceitful food.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Do not weary yourself to be rich. In your wisdom, show restraint.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Why do you set your eyes on that which is not? For it certainly sprouts wings like an eagle and flies in the sky.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Do not eat the food of him who has a stingy eye, and do not crave his delicacies:
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
for as he thinks about the cost, so he is. "Eat and drink." he says to you, but his heart is not with you.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
The morsel which you have eaten you shall vomit up, and lose your good words.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Do not speak in the ears of a fool, for he will despise the wisdom of your words.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Do not move the ancient boundary stone. Do not encroach on the fields of the fatherless:
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
for their Defender is strong. He will plead their case against you.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Apply your heart to instruction, and your ears to the words of knowledge.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Do not withhold correction from a child. If you punish him with the rod, he will not die.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
Punish him with the rod, and save his soul from Sheol. (Sheol )
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
My son, if your heart is wise, then my heart will be glad, even mine:
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
yes, my heart will rejoice, when your lips speak what is right.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Do not let your heart envy sinners; but rather fear the LORD all the day long.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
For surely there is a future, and your hope will not be cut off.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Listen, my son, and be wise, and keep your heart on the right path.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Do not be among ones drinking too much wine, or those who gorge themselves on meat:
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
for the drunkard and the glutton shall become poor; and drowsiness clothes them in rags.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Listen to your father who gave you life, and do not despise your mother when she is old.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Buy the truth, and do not sell it. Get wisdom, discipline, and understanding.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
The father of the righteous has great joy. Whoever fathers a wise child delights in him.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Let your father and your mother be glad. Let her who bore you rejoice.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
My son, give me your heart; and let your eyes keep in my ways.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
For a prostitute is a deep pit; and a wayward wife is a narrow well.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Yes, she lies in wait like a robber, and increases the unfaithful among men.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Who has woe? Who has sorrow? Who has strife? Who has complaints? Who has needless bruises? Who has bloodshot eyes?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Those who stay long at the wine; those who go to seek out mixed wine.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Do not look at the wine when it is red, when it sparkles in the cup, when it goes down smoothly.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
In the end, it bites like a serpent, and poisons like a viper.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Your eyes will see strange things, and your mind will imagine confusing things.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Yes, you will be as he who lies down in the midst of the sea, or as he who lies on top of the rigging:
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
"They hit me, and I was not hurt. They beat me, and I do not feel it. When will I wake up? I can do it again. I can find another."