< Miyambo 22 >
1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Din pa ye sen ahonya bebrebe; sɛ wobedi wo ni ye sen dwetɛ anaa sikakɔkɔɔ.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Ɔdefo ne ohiani wɔ ade baako, Awurade ne wɔn nyinaa Yɛfo.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Onitefo hu amanehunu a ɛreba na ohintaw ne ho, nanso atetekwaa kɔ nʼanim konya amane.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Ahobrɛase ne Awuradesuro ɛma ahonya ne anuonyam ne nkwa.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Nsɔe ne mfiri wɔ amumɔyɛfo akwan so, nanso nea ɔbɔ ne kra ho ban no mmɛn ho.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Kyerɛ abofra ɔkwan a ɔmfa so, na sɛ onyin a ɔremfi so.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Adefo di ahiafo so, na boseagyefo yɛ nea ɔde fɛm somfo.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Nea odua amumɔyɛsɛm no twa ɔhaw na wɔbɛsɛe nʼabufuwhyew abaa.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Ɔyamyefo benya nhyira efisɛ ɔne ahiafo kyɛ nʼaduan.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Pam ɔfɛwdifo na basabasayɛ nso bɛkɔ; ntɔkwaw ne animka to atwa.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Obi a ɔdɔ koma a mu tew na ne kasa ho yɛ nyam no, benya ɔhene afa no adamfo.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Awurade ani wɛn nimdeɛ, na ɔsɛe ɔtorofo nsɛm.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Ɔkwadwofo ka se, “Gyata bi wɔ mfikyiri hɔ!” anaasɛ, “Wobekum me wɔ mmɔnten so.”
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Ɔbea waresɛefo anom yɛ amoa donkudonku; nea ɔhyɛ Awurade abufuw ase no bɛtɔ mu.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Agyimisɛm kyekyere abofra koma ho, nanso nteɛso abaa bɛpam no akɔ akyiri.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Obi besisi ohiani de apɛ ahonya, anaa ɔbɛkyɛ ɔdefo ade, ne nyinaa de no kɔ ohia mu.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Yɛ aso na tie anyansasɛm yi; fa wo koma di me nkyerɛkyerɛ akyi,
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
efisɛ eye sɛ wokora saa nsɛm yi wɔ wo koma mu, na ne nyinaa ada wʼano.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Sɛ ɛbɛyɛ a wode wo ho bɛto Awurade so, merekyerɛkyerɛ wo nnɛ, yiw ɛyɛ wo.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Menkyerɛw mmɛ aduasa mmaa wo, nea ɛyɛ afotusɛm ne nimdeɛ,
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
a ɛkyerɛkyerɛ wo nokware ne nea akyinnye nni ho, sɛnea wubenya mmuae pa ama nea ɔsomaa wo no ana?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Mmɔ ahiafo korɔn, sɛ wɔyɛ ahiafo nti, na nsisi wɔn a wonni bi wɔ asennii,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
efisɛ Awurade bedi wɔn asɛm ama wɔn, na wafom afa wɔn a wɔfom ahiafo fa.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Mfa obi a ne koma yɛ den no adamfo, na mfa wo ho mmɔ nea ne bo nkyɛ fuw,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
anyɛ saa a, wubesua nʼakwan na woakɔtɔ afiri mu.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Nyɛ nea ɔde ne nsa hyɛ krataa ase di akagyinamu anaasɛ odi akagyinamu;
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
na sɛ wunni nea wɔde tua a wobehuam wo mpa mpo afi wʼase.
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Ntutu tete abo a wɔde ato hye, nea wo nenanom de sisii hɔ no.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Wuhu obi a ne nsa akokwaw nʼadwuma ho ana? Ahemfo anim na ɔbɛsom, na ɔrensom wɔ mpapahwekwa anim.