< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Tener una buena reputación es mejor que tener mucho dinero. El respeto es mejor que la plata y que el oro.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Los ricos y los pobres tienen algo en común: el Señor es su creador.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Si eres prudente, verás venir el peligro y te apartarás; pero los necios siguen sin cuidado y sufren las consecuencias.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Si eres humilde y respetas al Señor, tu recompense será la riqueza, el honor y la vida.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Solo hay espinas y trampas en el camino de los corruptos. Los que estiman sus vidas se mantendrán lejos de ellos.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Enseña a los niños el modo correcto de vivir, y cuando crezcan, seguirán viviendo en rectitud.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
El rico gobierna al pobre, y los que piden dinero prestado son esclavos de los prestamistas.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Los que siembran injusticia, cosecharán desastre. Y los golpes que dan a otros, cesarán.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Si eres generoso, serás bendecido por compartir tu comida con los necesitados.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Deshazte de los burlones y acabarás con el conflicto. Entonces no habrá discusiones ni insultos.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Todo el que estima la sinceridad y habla con cortesía, tendrá al rey como amigo.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
El Señor cuida del conocimiento, pero se opone a las palabras de los mentirosos.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Los perezosos dicen: “Hay un león allá afuera. ¡Si salgo podría morir!”
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Las palabras seductoras de una mujer inmoral son como una trampa peligrosa. Si el Señor está enojado contigo, caerás en la trampa.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Los niños son ignorantes por naturaleza. La corrección física les ayudará a entrar en razón.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Si oprimes al pobre para hacerte rico, o si eres generoso con el rico, terminarás siendo pobre tú mismo.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Atiende y escucha las palabras de los sabios. Medita cuidadosamente en mis enseñanzas,
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
porque es bueno que guardes estas palabras en tu mente para que estés listo para compartirlas.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Hoy te explico hoy para que confíes en el Señor. ¡Sí, a ti!
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
¿Acaso no he escrito para ti treinta consejos de sabiduría?
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
Son para aclararte lo recto y verdadero, a fin de que puedas dar una explicación veraz a aquellos a que te enviaron.
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Pues no debes robarle al pobre solo porque es pobre; y no deberías sofocar en la corte a los de menos recursos,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
porque el Señor peleará su caso, y recuperará lo que les hayan robado.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
No te hagas amigo de quien se enoja fácilmente. No se asocies con personas irascibles,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
para que no aprendas a ser como ellos y no destruyas tu vida.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
No te comprometas con apretón de manos a ser fiador de otro,
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
porque si no puedes pagar, ¿por qué tendrían que embargar tu cama?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
No muevas los hitos fronterizos que establecieron tus antepasados.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Si ves a alguien con talento en su trabajo, notarás que trabajará para reyes y no para la gente común.

< Miyambo 22 >