< Miyambo 22 >
1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Um bom nome é mais desejável do que grandes riquezas, e favor amoroso é melhor do que prata e ouro.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Os ricos e os pobres têm isso em comum: Yahweh é o criador de todos eles.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Um homem prudente vê o perigo e se esconde; mas o simples passar adiante, e sofrer por ele.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
O resultado da humildade e do medo de Yahweh é riqueza, honra e vida.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Espinhos e laços estão no caminho dos malvados; quem guarda sua alma, fica deles.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Treinar uma criança no caminho que ela deve seguir, e quando ele for velho, não se afastará dele.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Os ricos dominam sobre os pobres. O tomador do empréstimo é servo do doador.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
He que semeia a maldade colhe problemas, e a haste de sua fúria será destruída.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Aquele que tiver um olho generoso será abençoado, pois ele compartilha sua comida com os pobres.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Expulsar o escarnecedor, e a briga sairá; sim, as brigas e insultos vão parar.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Aquele que ama a pureza de coração e fala graciosamente é o amigo do rei.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Os olhos de Yahweh zelam pelo conhecimento, mas ele frustra as palavras dos infiéis.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
O preguiçoso diz: “Há um leão lá fora! Eu serei morto nas ruas”!
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
A boca de uma adúltera é um poço profundo. Aquele que está sob a ira de Yahweh cairá nela.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
A loucura está ligada ao coração de uma criança; a vara da disciplina o afasta dele.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Quem oprime os pobres por seu próprio aumento e quem dá aos ricos, ambos chegam à pobreza.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Vire seu ouvido, e ouça as palavras dos sábios. Aplique seu coração ao meu ensino.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
Pois é uma coisa agradável se você os mantiver dentro de você, se todos eles estiverem prontos em seus lábios.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Eu lhes ensino hoje, até mesmo vocês, para que sua confiança possa estar em Yahweh.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Não lhe escrevi trinta coisas excelentes de conselhos e conhecimentos,
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
Para lhe ensinar a verdade, palavras confiáveis, para dar boas respostas àqueles que o enviaram?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Não explore os pobres porque ele é pobre; e não esmague os necessitados no tribunal;
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
para Yahweh defenderá seu caso, e saqueia a vida daqueles que os saqueiam.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Não seja amigo de um homem de temperamento quente. Não se associe com alguém que guarda a raiva,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
para que você não aprenda seus caminhos e ludibriar sua alma.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Não seja um daqueles que batem as mãos, daqueles que são garantia de dívidas.
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Se você não tiver meios para pagar, por que ele deveria tirar sua cama de baixo de você?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Não mova a antiga pedra de fronteira que seus pais criaram.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Do você vê um homem hábil em seu trabalho? Ele servirá aos reis. Ele não servirá a homens obscuros.