< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Ibizo elihle likhethekile kulenotho enengi; isisa esihle kulesiliva njalo kulegolide.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Onothileyo lomyanga bayahlangana; iNkosi yabenza bonke.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Ohlakaniphileyo ubona ububi acatshe, kodwa abangelalwazi bayaqhubeka babesebejeziswa.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Umvuzo wokuthobeka lokwesaba iNkosi kuyinotho lodumo lempilo.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Ameva lemijibila kusendleleni yabaphambeneyo; ogcina umphefumulo wakhe uzakuba khatshana labo.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Fundisa umntwana endleleni angahamba ngayo; ngitsho esemdala kayikuphambuka kuyo.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Onothileyo ubusa abayanga, lomeboleki uyisigqili somebolekisi.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Ohlanyela ukonakala uzavuna ukuhlupheka, lentonga yolaka lwakhe izaphela.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Olelihlo elilokuhle yena uzabusiswa, ngoba unikile okwesinkwa sakhe kumyanga.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Xotsha isideleli, kuzaphuma lenkani, yebo, ingxabano lehlazo kuzaphela.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Othanda ukuhlanzeka kwenhliziyo, ngenxa yesisa sendebe zakhe, inkosi ingumgane wakhe.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Amehlo eNkosi alondoloza ulwazi, kodwa izachitha amazwi abangathembekanga.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Ivila lithi: Kulesilwane ngaphandle; ngizabulawa phakathi kwezitalada.
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Umlomo wabesifazana bemzini ungumgodi otshonayo; lowo iNkosi emthukutheleleyo uzawela khona.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Ubuthutha bubotshelwe enhliziyweni yomntwana; uswazi lokuqondisa luzabususela khatshana laye.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Ocindezela umyanga ukwandisa alakho, opha onothileyo, isibili uzakuba ngoswelayo.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Beka indlebe yakho, uzwe amazwi abahlakaniphileyo, umise inhliziyo yakho elwazini lami.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
Ngoba kumnandi uba uwalondoloza emibilini yakho; azahlala elungile kanyekanye endebeni zakho.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Ukuze ithemba lakho libe seNkosini, ngikwazisile wona lamuhla, ngitsho wena.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Kangikubhalelanga yini izinto ezinhle kakhulu kuzeluleko lelwazini?
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
Ukukwazisa ukuqiniseka kwamazwi eqiniso, ukuze ubuyisele amazwi eqiniso kulabo abakuthumileyo.
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Ungamphangi umyanga ngoba engumyanga, njalo ungamchobozi oswelayo esangweni.
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
Ngoba iNkosi izamela udaba lwabo, iphange umphefumulo wababaphangayo.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Ungahlanganyeli lomuntu ololaka, ungahambisani lomuntu othukuthelayo,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
hlezi ufunde indlela zakhe, wemukele umjibila emphefumulweni wakho.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Ungabi phakathi kwababambana izandla, phakathi kwabayizibambiso ngezikwelede.
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Uba ungelakho okokuhlawula, kungani ezathatha umbheda wakho ngaphansi kwakho?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Ungatshedisi isikhonkwane esidala somngcele, oyihlo abasenzayo.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Uyambona yini umuntu oyingcitshi emsebenzini wakhe? Uzazimisa phambi kwamakhosi; kayikuzimisa phambi kwabantukazana.

< Miyambo 22 >