< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Melius est nomen bonum, quam divitiae multae: super argentum et aurum, gratia bona.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Dives, et pauper obviaverunt sibi: utriusque operator est Dominus.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Callidus videt malum, et abscondit se: innocens pertransiit, et afflictus est damno.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Finis modestiae timor Domini, divitiae et gloria et vita.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Arma et gladii in via perversi: custos autem animae suae longe recedit ab eis.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Proverbium est: Adolescens iuxta viam suam, etiam cum senuerit, non recedet ab ea.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Dives pauperibus imperat: et qui accipit mutuum, servus est foenerantis.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Qui seminat iniquitatem, metet mala, et virga irae suae consummabitur.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Qui pronus est ad misericordiam, benedicetur: de panibus enim suis dedit pauperi. Victoriam et honorem acquiret qui dat munera: animam autem aufert accipientium.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Eiice derisorem, et exibit cum eo iurgium, cessabuntque causae et contumeliae.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Qui diligit cordis munditiam, propter gratiam labiorum suorum habebit amicum regem.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Oculi Domini custodiunt scientiam: et supplantantur verba iniqui.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Dicit piger: Leo est foris, in medio platearum occidendus sum.
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Fovea profunda, os alienae: cui iratus est Dominus, incidet in eam.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Stultitia colligata est in corde pueri, et virga disciplinae fugabit eam.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Qui calumniatur pauperem, ut augeat divitias suas, dabit ipse ditiori, et egebit.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Fili mi! Inclina aurem tuam, et audi verba sapientium: appone autem cor ad doctrinam meam.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
quae pulchra erit tibi, cum servaveris eam in ventre tuo, et redundabit in labiis tuis:
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Ut sit in Domino fiducia tua, unde et ostendi eam tibi hodie.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Ecce descripsi eam tibi tripliciter, in cogitationibus et scientia:
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
ut ostenderem tibi firmitatem, et eloquia veritatis, respondere ex his illis, qui miserunt te.
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Non facias violentiam pauperi, quia pauper est: neque conteras egenum in porta:
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
quia iudicabit Dominus causam eius, et configet eos, qui confixerunt animam eius.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Noli esse amicus homini iracundo, neque ambules cum viro furioso:
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
ne forte discas semitas eius, et sumas scandalum animae tuae.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Noli esse cum his, qui defigunt manus suas, et qui vades se offerunt pro debitis:
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
si enim non habes unde restituas, quid causae est ut tollat operimentum de cubili tuo?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Ne transgrediaris terminos antiquos, quos posuerunt patres tui.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Vidisti virum velocem in opere suo? coram regibus stabit, nec erit ante ignobiles.

< Miyambo 22 >