< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Yon bon non pi bon pase tout richès; e favè Bondye, pase ajan ak lò.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Rich la ak malere a mare ansanm; se SENYÈ a ki fè yo tout.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Sila ki reflechi, wè mal e kache kò li; men ensanse yo antre ladann e jwenn pinisyon.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Rekonpans pou imilite avèk lakrent SENYÈ a se richès, bon repitasyon, ak lavi.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Pikan ak pèlen se nan chemen a pèvès yo; sila ki veye nanm li, va rete lwen yo.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Leve yon timoun nan chemen li ta dwe ale, e lè li vin gran, li p ap kite li; menm lè l granmoun, li p ap kite li.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Rich yo domine sou pòv yo, e moun ki prete vin esklav a sila k ap bay prè a.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Sila ki simen inikite a va rekòlte vanite; e baton kòlè li a va detwi.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Sila ki bay ak men louvri va beni; paske li bay manje a malere.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Mete moun k ap moke moun yo deyò, e diskisyon an prale tou; wi, konfli ak dezonore moun ap sispann.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Sila ki renmen kè ki san tach e ki pale ak gras, va zanmi a wa a.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Zye a SENYÈ a konsève konesans; men Li boulvèse pawòl moun malveyan yo.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Parese a di: “Gen yon lyon deyò a; m ap mouri nan lari!”
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Bouch a fanm adiltè a se yon fòs byen fon; sila ke SENYÈ a modi va tonbe ladann.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Foli mare nan kè a yon timoun; baton disiplin nan va retire sa mete lwen li.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Sila ki oprime malere a pou ogmante tèt li; ni sila k ap fè kado a rich yo, va rive nan povrete.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Apiye zòrèy ou pou tande pawòl a saj yo; epi aplike ou a konesans mwen.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
Paske sa va byen agreyab pou ou si ou kenbe yo anndan ou, pou yo toujou prè sou lèv ou.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Pou konfyans ou kapab nan SENYÈ a, mwen te enstwi ou jodi a, menm ou menm nan.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Èske mwen pa t ekri ou trant bèl bagay, de konsèy ak konesans yo?
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
Pou fè ou konnen vrè pawòl verite yo, pou ou kab byen reponn sila ki te voye ou a?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Pa vòlè malere a paske li pòv, ni kraze aflije nan pòtay la;
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
paske, SENYÈ a va plede ka yo e pran lavi a sila ki vòlè yo.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Pa asosye ak yon nonm ki livre a kòlè; oswa ale ak yon moun kolerik,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
sinon, ou va aprann mès li yo e jwenn yon pèlen pou tèt ou.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Pa konte pami sila ki sèvi kon garanti yo, pami sila ki fè sekirite pou dèt yo.
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Si ou pa gen mwayen pou ou kab peye, poukisa ou ta kite l rale kabann nan sòti anba ou?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Pa deplase ansyen bòn ke papa zansèt nou yo te mete a.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Èske ou wè yon nonm byen abil nan travay li? Li va kanpe devan wa yo; li p ap oblije kanpe devan nenpòt kalite vye moun.

< Miyambo 22 >