< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Un nom estimé est préférable à la grande richesse: la sympathie est plus précieuse que l’argent et que l’or.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Riche et pauvre sont sur la même ligne: l’Eternel les a faits l’un et l’autre.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
L’Homme avisé aperçoit le danger et se met à l’abri; les niais passent outre et en pâtissent.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Fruits de l’humilité, de la crainte de Dieu: richesse, honneur et vie!
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Des lacets et des pièges sont semés sur la route du pervers; qui tient à sa vie s’en éloigne.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Donne au jeune homme de bonnes habitudes dès le début de sa carrière; même avancé en âge, il ne s’en écartera point.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Le riche prime les pauvres; le débiteur est prisonnier de son créancier.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Qui sème l’injustice, récolte l’adversité, l’instrument de sa passion sera anéanti.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Celui qui a bon cœur sera béni, car il partage son pain avec le pauvre.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Expulse le persifleur, la discorde décampera avec lui, plus de disputes ni d’injures!
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Un ami au cœur pur, par l’agrément de ses lèvres, gagne l’affection du roi.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Les yeux de l’Eternel protègent le vrai savoir; mais ils renversent les entreprises du perfide.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Le paresseux s’écrie: "Il y a un lion dehors! Je vais être massacré en pleine rue!"
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
La bouche des femmes étrangères est comme un abîme profond; celui que Dieu réprouve y tombe.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
La sottise est attachée au cœur de l’adolescent; la verge qui châtie doit l’en arracher.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
On pressure le pauvre, et cela tourne à son profit; on donne au riche, et c’est un appauvrissement pour lui.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Incline ton oreille et écoute les paroles des sages; prête ton attention aux leçons de mon expérience.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
II sera beau pour toi de les retenir en ton cœur, de les fixer en permanence sur tes lèvres.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Mets ta confiance en l’Eternel; voilà ce que je t’enseigne à toi-même en ce jour.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
N’Est-ce pas à ton intention que j’ai consigné par écrit d’importantes maximes, en fait de bons conseils et d’expérience,
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
pour t’apprendre ce qu’iI y a de réel dans les dictons de la vérité et te permettre de présenter fidèlement les choses à ceux qui t’envoient?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Ne dépouille pas le faible parce qu’il est sans défense; n’écrase pas le pauvre à la Porte,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
car l’Eternel prend en mains leur cause et il traite avec rigueur ceux qui leur infligent des vexations.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Ne fraye pas avec un homme irascible, ne lie pas société avec quelqu’un qui s’emporte:
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
tu pourrais copier leurs mœurs et t’engager toi-même dans un piège.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Ne sois pas de ceux qui disent: "Touchez-là!" et qui se portent garants pour des emprunts.
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Que tu n’aies pas de quoi payer, pourquoi t’exposer à ce que l’on saisisse la couche où tu reposes?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Ne déplace pas les bornes antiques, que tes pères ont posées.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Vois cet homme diligent dans son travail: il pourra paraître devant les rois au lieu de se tenir auprès des gens obscurs.

< Miyambo 22 >